< Yesaya 57 >

1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
The righteous man perishes, and no man lays it to heart. And merciful men are taken away; none considering that the righteous man is taken away from the evil.
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
He enters into peace. They rest in their beds, each one who walks in his uprightness.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
But draw near here, ye sons of the sorceress, the seed of the adulterer and the harlot.
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Against whom do ye sport yourselves, against whom ye make a wide mouth, and put out the tongue? Are ye not children of transgression, a seed of falsehood,
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
ye who inflame yourselves among the oaks, under every green tree, who kill the children in the valleys, under the clefts of the rocks?
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Among the smooth stones of the valley is thy portion. They, they are thy lot, even to them thou have poured a drink offering; thou have offered an oblation. Shall I be appeased for these things?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Upon a high and lofty mountain thou have set thy bed. Thou also went up there to offer sacrifice.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
And behind the doors and the posts thou have set up thy memorial. For thou have uncovered thyself to another than me, and have gone up. Thou have enlarged thy bed, and made thee a covenant with them. Thou loved their bed where thou saw it.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
And thou went to the king with oil, and increased thy perfumes, and sent thine ambassadors far off, and debased thyself even to Sheol. (Sheol h7585)
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
Thou were wearied with the length of thy way, yet thou did not say, It is in vain. Thou found a quickening of thy strength, therefore thou were not faint.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
And of whom have thou been afraid and in fear, that thou lie, and have not remembered me, nor laid it to thy heart? Have I not held my peace even of long time, and thou do not fear me?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
I will declare thy righteousness. And as for thy works, they shall not profit thee.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
When thou cry, let those whom thou have gathered deliver thee. But the wind shall take them; a breath shall carry them all away. But he who takes refuge in me shall possess the land, and shall inherit my holy mountain.
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
And he will say, Cast ye up, cast ye up, prepare the way. Take up the stumbling-block out of the way of my people.
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
For thus says the high and lofty One who inhabits eternity, whose name is Holy: I dwell in the high and holy place, also with him who is of a contrite and humble spirit, to revive the spirit of the humble, and to revive the heart of the contrite.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
For I will not contend forever, nor will I always be angry, for the spirit would faint before me, and the souls that I have made.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
For the iniquity of his covetousness I was angry, and smote him. I hid my face and was angry, and he went on backsliding in the way of his heart.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
I have seen his ways, and will heal him. I will lead him also, and restore comforts to him and to his mourners.
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
I create the fruit of the lips. Peace, peace, to him who is far off and to him who is near, says Jehovah, and I will heal him.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
But the wicked are like the troubled sea, for it cannot rest, and its waters cast up mire and dirt.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
There is no peace, says my God, to the wicked.

< Yesaya 57 >