< Yesaya 51 >

1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
Hearken to me, ye who follow after righteousness, ye who seek Jehovah. Look to the rock from where ye were hewn, and to the hold of the pit from where ye were dug.
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Look to Abraham your father, and to Sarah who bore you. For when he was but one I called him, and I blessed him, and made him many.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
For Jehovah has comforted Zion. He has comforted all her waste places, and has made her wilderness like Eden, and her desert like the garden of Jehovah. Joy and gladness shall be found therein, thanksgiving, and the voice of melody.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
Attend to me, O my people, and give ear to me, O my nation. For a law shall go forth from me, and I will establish my justice for a light of the peoples.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
My righteousness is near. My salvation has gone forth, and my arms shall judge the peoples. The isles shall wait for me, and on my arm they shall trust.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Lift up your eyes to the heavens, and look upon the earth beneath. For the heavens shall vanish away like smoke, and the earth shall grow old like a garment, and those who dwell in it shall die in like manner. But my salvation shall be forever, and my righteousness shall not be abolished.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
Hearken to me, ye who know righteousness, the people in whose heart is my law. Fear ye not the reproach of men, nor be ye dismayed at their revilings.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
For the moth shall eat them up like a garment, and the worm shall eat them like wool. But my righteousness shall be forever, and my salvation to all generations.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Awake, awake, put on strength, O arm of Jehovah. Awake, as in the days of old, the generations of ancient times. Is it not thou who cut Rahab in pieces, who pierced the monster?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
Is it not thou who dried up the sea, the waters of the great deep, who made the depths of the sea a way for the redeemed to pass over?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
And the ransomed of Jehovah shall return, and come with singing to Zion, and everlasting joy shall be upon their heads. They shall obtain gladness and joy, and sorrow and sighing shall flee away.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
I, even I, am he who comforts you. Who are thou, that thou are afraid of man who shall die, and of the son of man who shall be made as grass,
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
and have forgotten Jehovah thy maker, who stretched forth the heavens, and laid the foundations of the earth, and fear continually all the day because of the fury of the oppressor, when he makes ready to destroy? And where is the fury of the oppressor?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
The captive exile shall speedily be loosed, and he shall not die in the pit, nor shall his bread fail.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
For I am Jehovah thy God, who stirs up the sea so that the waves of it roar. Jehovah of hosts is his name.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
And I have put my words in thy mouth, and have covered thee in the shadow of my hand, that I may plant the heavens, and lay the foundations of the earth, and say to Zion, Thou are my people.
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
Awake, awake, stand up, O Jerusalem, who have drunk at the hand of Jehovah the cup of his wrath. Thou have drunk the bowl of the cup of staggering, and drained it.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
There is none to guide her among all the sons whom she has brought forth, nor is there any who takes her by the hand among all the sons that she has brought up.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
These two things have befallen thee (Who shall bemoan thee?): Desolation and destruction, and the famine and the sword. How shall I comfort thee?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Thy sons have fainted. They lie at the head of all the streets, as an antelope in a net. They are full of the wrath of Jehovah, the rebuke of thy God.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Therefore hear now this, thou afflicted, and drunken, but not with wine.
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Thus says thy lord Jehovah, and thy God who pleads the cause of his people: Behold, I have taken out of thy hand the cup of staggering, even the bowl of the cup of my wrath. Thou shall no more drink it again.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
And I will put it into the hand of those who afflict thee, who have said to thy soul, Bow down, that we may go over, and thou have laid thy back as the ground, and as the street, to those who go over.

< Yesaya 51 >