< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
The Song of songs, which is Solomon's.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Let him kiss me with the kisses of his mouth, for thy love is better than wine.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Thine oils have a good fragrance. Thy name is oil poured forth. Therefore the virgins love thee.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Draw me, we will run after thee. The king has brought me into his chambers. We will be glad and rejoice in thee. We will make mention of thy love more than of wine. Rightly do they love thee.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
I am black, but comely, O ye daughters of Jerusalem, as the tents of Kedar, as the curtains of Solomon.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Look not upon me, because I am swarthy, because the sun has scorched me. My mother's sons were incensed against me. They made me keeper of the vineyards, but my own vineyard I have not kept.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Tell me, O thou whom my soul loves, where thou feed thy flock, where thou make it to rest at noon. For why should I be as she who is veiled beside the flocks of thy companions?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
If thou know not, O thou fairest among women, go thy way forth by the footsteps of the flock, and feed thy kids beside the shepherds' tents.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
I have compared thee, O my love, to a steed in Pharaoh's chariots.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Thy cheeks are comely with plaits of hair, thy neck with strings of jewels.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
We will make thee plaits of gold with studs of silver.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
While the king sat at his table, my spikenard sent forth its fragrance.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
My beloved is to me a bundle of myrrh that lies between my breasts.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
My beloved is to me a cluster of henna-flowers in the vineyards of En-gedi.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Behold, thou are fair, my love, behold thou are fair. Thine eyes are doves.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Behold, thou are fair, my beloved, yea, pleasant. Also our couch is green.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
The beams of our house are cedars, our rafters are firs.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >