< Yesaya 52 >

1 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
Awake, awake, put on thy strength, O Zion. Put on thy beautiful garments, O Jerusalem, the holy city. For henceforth there shall no more come into thee the uncircumcised and the unclean.
2 Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
Shake thyself from the dust. Arise, sit up, O Jerusalem. Loose thyself from the bonds of thy neck, O captive daughter of Zion.
3 Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
For thus says Jehovah: Ye were sold for nothing, and ye shall be redeemed without money.
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
For thus says the lord Jehovah, My people went down at the first into Egypt to sojourn there. And the Assyrian has oppressed them without cause.
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
Now therefore, what do I do here, says Jehovah, seeing that my people are taken away for nothing? Those who rule over them howl, says Jehovah, and because of you my name is continually blasphemed among the Gentiles.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
Therefore my people shall know my name. Therefore they shall know in that day that I am he who speaks, Behold, it is I.
7 Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
How beautiful upon the mountains are the feet of him who brings good news, who publishes peace, who brings good news of good, who publishes salvation, who says to Zion, Thy God reigns!
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
The voice of thy watchmen! They lift up the voice; they sing together. For they shall see eye to eye, when Jehovah returns to Zion.
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
Break forth into joy, sing together, ye waste places of Jerusalem, for Jehovah has comforted his people. He has redeemed Jerusalem.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Jehovah has made bare his holy arm in the eyes of all the nations, and all the ends of the earth have seen the salvation of our God.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
Depart ye, depart ye, go ye out from there. Touch no unclean thing. Go ye out of the midst of her. Cleanse yourselves, ye who bear the vessels of Jehovah.
12 Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
For ye shall not go out in haste, nor shall ye go by flight. For Jehovah will go before you, and the God of Israel will be your rearward.
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
Behold, my servant shall deal wisely. He shall be exalted and lifted up, and shall be very high.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
Just as many were astonished at thee (his visage was so marred, more than any man, and his form more than the sons of men),
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
so shall he sprinkle many nations. Kings shall shut their mouths at him. For that which had not been told them they shall see, and that which they had not heard they shall understand.

< Yesaya 52 >