< Yesaya 53 >

1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Who has believed our report? And to whom has the arm of Jehovah been revealed?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
For he grew up before him as a tender plant, and as a root out of a dry ground. He has no form nor comeliness. And when we see him, there is no beauty that we should desire him.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
He was despised, and rejected by men, a man of sorrows, and acquainted with grief. And as him from whom men hide their face he was despised, and we esteemed him not.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
Surely he has borne our griefs, and carried our sorrows. Yet we esteemed him stricken, smitten by God, and afflicted.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
But he was wounded for our transgressions. He was bruised for our iniquities. The chastisement of our peace was upon him, and with his stripes we are healed.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
All we like sheep have gone astray. We have turned every one to his own way, and Jehovah has laid on him the iniquity of us all.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
He was oppressed, yet when he was afflicted he opened not his mouth. As a lamb that is led to the slaughter, and as a sheep that is mute before its shearers, so he opened not his mouth.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
In his humiliation his justice was taken away. And as for his generation, who considered that he was cut off out of the land of the living for the transgression of my people, to whom the stroke was due?
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
And they made his grave with the wicked, and with a rich man in his death. Although he had done no violence, nor was any deceit in his mouth.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Yet it pleased Jehovah to bruise him. He has put him to grief. When thou shall make his soul an offering for sin, he shall see his seed. He shall prolong his days, and the pleasure of Jehovah shall prosper in his hand.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
He shall see of the travail of his soul, and shall be satisfied. By the knowledge of himself shall my righteous servant justify many, and he shall bear their iniquities.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Therefore I will divide him a portion with the great, and he shall divide the spoil with the strong, because he poured out his soul to death, and was numbered with the transgressors. Yet he bore the sin of many, and made intercession for the transgressors.

< Yesaya 53 >