< Yesaya 56 >

1 Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
Thus says Jehovah, Keep ye justice, and do righteousness. For my salvation is near to come, and my righteousness to be revealed.
2 Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
Blessed is the man who does this, and the son of man who holds it fast, who keeps the sabbath from profaning it, and keeps his hand from doing any evil.
3 Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
Neither let the foreigner, who has joined himself to Jehovah, speak, saying, Jehovah will surely separate me from his people, nor let the eunuch say, Behold, I am a dry tree.
4 Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
For thus says Jehovah of the eunuchs who keep my sabbaths, and choose the things that please me, and hold fast my covenant:
5 ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
To them I will give in my house and within my walls a memorial and a name better than of sons and of daughters. I will give them an everlasting name, that shall not be cut off.
6 Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
Also the foreigners who join themselves to Jehovah, to minister to him, and to love the name of Jehovah, to be his servants, everyone who keeps the sabbath from profaning it, and holds fast my covenant,
7 amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
even them I will bring to my holy mountain, and make them joyful in my house of prayer. Their burnt offerings and their sacrifices shall be accepted upon my altar, for my house shall be called a house of prayer for all peoples.
8 Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
The lord Jehovah, who gathers the outcasts of Israel, says, Yet I will gather to him, besides his own who are gathered.
9 Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
All ye beasts of the field, come to devour, yea, all ye beasts in the forest.
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
His watchmen are blind. They are all without knowledge. They are all mute dogs. They cannot bark, dreaming, lying down, loving to slumber.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
Yea, the dogs are greedy; they can never have enough. And these are shepherds who cannot understand. They have all turned to their own way, each one to his gain, from every quarter.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”
Come ye, they say, I will fetch wine, and we will fill ourselves with strong drink. And tomorrow shall be as this day, great beyond measure.

< Yesaya 56 >