< Yesaya 58 >

1 “Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
Cry aloud, spare not. Lift up thy voice like a trumpet, and declare to my people their transgression, and to the house of Jacob their sins.
2 Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
Yet they seek me daily, and delight to know my ways. As a nation that did righteousness, and forsook not the ordinance of their God, they ask of me righteous judgments; they delight to draw near to God.
3 Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
Why have we fasted, they say, and thou see not? We have afflicted our soul, and thou take no knowledge. Behold, in the day of your fast ye find pleasure, and exact from all your laborers.
4 Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Behold, ye fast for strife and contention, and to smite with the fist of wickedness. Ye do not fast this day so as to make your voice to be heard on high.
5 Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
Is such the fast that I have chosen, the day for a man to afflict his soul? Is it to bow down his head as a rush, and to spread sackcloth and ashes under him? Will thou call this a fast, and an acceptable day to Jehovah?
6 “Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
Is not this the fast that I have chosen: to loose the bonds of wickedness, to undo the bands of the yoke, and to let the oppressed go free, and that ye break every yoke?
7 Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
Is it not to deal thy bread to a hungry man, and that thou bring the poor who are cast out to thy house, when thou see a naked man, that thou cover him, and that thou not hide thyself from thine own flesh?
8 Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
Then thy light shall break forth as the morning, and thy healing shall spring forth speedily. And thy righteousness shall go before thee. The glory of Jehovah shall be thy rearward.
9 Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
Then thou shall call, and Jehovah will answer, thou shall cry, and he will say, Here I am. If thou take the yoke away from the midst of thee, the putting forth of the finger, and speaking wickedly,
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
and if thou draw out thy soul to a hungry man, and satisfy an afflicted soul, then thy light shall rise in darkness, and thine obscurity be as the noonday.
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
And Jehovah will guide thee continually, and satisfy thy soul in dry places, and make strong thy bones. And thou shall be like a watered garden, and like a spring of water whose waters fail not.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
And those who shall be of thee shall build the old waste places. Thou shall raise up the foundations of many generations, and thou shall be called The repairer of the breach, The restorer of paths to dwell in.
13 “Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
If thou turn away thy foot from the sabbath, from doing thy pleasure on my holy day, and call the sabbath a delight, and the holy of Jehovah honorable, and shall honor it, not doing thine own ways, nor finding thine own pleasure, nor speaking thine own words:
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.
then thou shall delight thyself in Jehovah, and I will make thee to ride upon the high places of the earth, and I will feed thee with the heritage of Jacob thy father. For the mouth of Jehovah has spoken it.

< Yesaya 58 >