< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
But now thus says Jehovah who created thee, O Jacob, and he who formed thee, O Israel: Fear not, for I have redeemed thee. I have called thee by thy name, Thou are mine.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
When thou pass through the waters, I will be with thee, and through the rivers, they shall not overflow thee. When thou walk through the fire, thou shall not be burned, nor shall the flame kindle upon thee.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
For I am Jehovah thy God, the Holy One of Israel, thy Savior. I have given Egypt as thy ransom, Ethiopia and Seba in thy stead.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Since thou have been precious in my sight, and honorable, and I have loved thee, therefore I will give men in thy stead, and peoples instead of thy life.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Fear not, for I am with thee. I will bring thy seed from the east, and gather thee from the west.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
I will say to the north, Give up, and to the south, Keep not back. Bring my sons from far, and my daughters from the end of the earth,
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
everyone who is called by my name, and whom I have created for my glory, whom I have formed, yea, whom I have made.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Bring forth the blind people who have eyes, and the deaf who have ears.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Let all the nations be gathered together, and let the peoples be assembled. Who among them can declare this, and show us former things? Let them bring their witnesses that they may be justified, or let them hear, and say, It is truth.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Ye are my witnesses, says Jehovah, and my servant whom I have chosen, that ye may know and believe me, and understand that I am he. Before me there was no God formed, nor shall there be after me.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
I, even I, am Jehovah, and besides me there is no savior.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
I have declared, and I have saved, and I have shown, and there was no strange god among you. Therefore ye are my witnesses, says Jehovah, and I am God.
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
Yea, since the day was I am he, and there is none that can deliver out of my hand. I will work, and who can hinder it?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Thus says Jehovah, your Redeemer, the Holy One of Israel: For your sake I have sent to Babylon, and I will bring down all of them as fugitives, even the Chaldeans, in the ships of their rejoicing.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
I am Jehovah, your Holy One, the Creator of Israel, your King.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
Thus says Jehovah, who makes a way in the sea, and a path in the mighty waters,
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
who brings forth the chariot and horse, the army and the mighty man (they lie down together; they shall not rise; they are extinct; they are quenched as a wick):
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Do not remember ye the former things, nor consider the things of old.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Behold, I will do a new thing. Now it shall spring forth. Shall ye not know it? I will even make a way in the wilderness, and rivers in the desert.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
The beasts of the field shall honor me, the jackals and the ostriches, because I give waters in the wilderness, and rivers in the desert, to give drink to my people, my chosen,
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
the people whom I formed for myself, that they might set forth my praise.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
Yet thou have not called upon me, O Jacob, but thou have been weary of me, O Israel.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Thou have not brought me from thy sheep for burnt offerings, nor have thou honored me with thy sacrifices. I have not burdened thee with offerings, nor wearied thee with frankincense.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Thou have bought me no sweet cane with money, nor have thou filled me with the fat of thy sacrifices. But thou have burdened me with thy sins. Thou have wearied me with thine iniquities.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
I, even I, am he who blots out thy transgressions for my own sake, and I will not remember thy sins.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Put me in remembrance. Let us plead together. Set thou forth thy case that thou may be justified.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Thy first father sinned, and thy teachers have transgressed against me.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
Therefore I will profane the rulers of the sanctuary, and I will make Jacob a curse, and Israel a reviling.

< Yesaya 43 >