< Yesaya 42 >

1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
Behold, my servant, whom I uphold, my chosen, in whom my soul delights. I have put my Spirit upon him, he will bring forth justice to the Gentiles.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
He will not cry, nor lift up his voice, nor cause it to be heard in the street.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
A bruised reed he will not break, and a dimly burning wick he will not quench, but he will bring forth justice in truth.
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
He will not fail nor be discouraged till he has set justice in the earth. And in his name Gentiles will hope.
5 Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
Thus says God, Jehovah, he who created the heavens, and stretched them forth, he who spread abroad the earth and that which comes out of it, he who gives breath to the people upon it, and spirit to those who walk in it,
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
I, Jehovah, have called thee in righteousness, and will hold thy hand, and will keep thee, and give thee for a covenant of the people, for a light of the Gentiles,
7 Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
to open the blind eyes, to bring out the prisoners from the dungeon, and those who sit in darkness out of the prison-house.
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
I am Jehovah. That is my name, and I will not give my glory to another, nor my praise to graven images.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
Behold, the former things have come to pass, and I declare new things. Before they spring forth I tell you of them.
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
Sing to Jehovah a new song, and his praise from the end of the earth, ye who go down to the sea, and all that is therein, the isles, and the inhabitants thereof.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
Let the wilderness and the cities of it lift up their voice, the villages that Kedar inhabits. Let the inhabitants of Sela sing. Let them shout from the top of the mountains.
12 Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
Let them give glory to Jehovah, and declare his praise in the islands.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
Jehovah will go forth as a mighty man. He will stir up his zeal like a man of war. He will cry, yea, he will shout aloud. He will do mightily against his enemies.
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
I have for a long time held my peace. I have been still, and refrained myself. Now I will cry out like a travailing woman. I will gasp and pant together.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
I will lay waste mountains and hills, and dry up all their herbs. And I will make the rivers islands, and will dry up the pools.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
And I will bring the blind by a way that they know not. I will lead them in paths that they know not. I will make darkness light before them, and crooked places straight. These things I will do, and I will not forsake them.
17 Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
They shall be turned back, they shall be utterly put to shame, who trust in graven images, who say to molten images, Ye are our gods.
18 “Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
Hear, ye deaf, and look, ye blind, that ye may see.
19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
Who is blind, but my servant, or deaf, as my messenger that I send? Who is blind as he who is at peace with me, and blind as Jehovah's servant?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
Thou see many things, but thou do not observe. His ears are open, but he does not hear.
21 Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
It pleased Jehovah, for his righteousness' sake, to magnify the law, and make it honorable.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
But this is a people robbed and plundered. They are all of them snared in holes, and they are hid in prison-houses. They are for a prey, and none delivers, for a spoil, and none says, Restore.
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
Who is there among you that will give ear to this, that will hearken and hear for the time to come?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
Who gave Jacob for a spoil, and Israel to the robbers? Did not Jehovah? He against whom we have sinned, and in whose ways they would not walk, nor were they obedient to his law.
25 Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
Therefore he poured upon him the fierceness of his anger, and the strength of battle. And it set him on fire round about, yet he knew not. And it burned him, yet he laid it not to heart.

< Yesaya 42 >