< Yesaya 41 >

1 “Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
Keep silence before me, O islands, and let the peoples renew their strength. Let them come near, then let them speak. Let us come near together to judgment.
2 “Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
Who raised up the righteous man from the east, calls him to his foot, gives nations before him, and makes him rule over kings? He gives them as the dust to his sword, as the driven stubble to his bow.
3 Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
He pursues them, and passes on safely, even by a way that he had not gone with his feet.
4 Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
Who has wrought and done it, calling the generations from the beginning? I, Jehovah, the first, and with the last, I am he.
5 Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
The isles have seen, and fear. The ends of the earth tremble, they draw near, and come.
6 aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
They help every man his neighbor, and says to his brother, Be of good courage.
7 Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
So the carpenter encourages the goldsmith, he who smoothes with the hammer, him who smites the anvil, saying of the soldering, It is good, and he fastens it with nails, that it should not be moved.
8 “Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
But thou, Israel, my servant, Jacob whom I have chosen, the seed of Abraham my friend,
9 Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
thou whom I have taken hold of from the ends of the earth, and called from the corners thereof, and said to thee, Thou are my servant, I have chosen thee and not cast thee away.
10 Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
Fear thou not, for I am with thee. Be not dismayed, for I am thy God. I will strengthen thee. Yea, I will help thee. Yea, I will uphold thee with the right hand of my righteousness.
11 “Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
Behold, all those who are incensed against thee shall be put to shame and confounded. Those who strive with thee shall be as nothing, and shall perish.
12 Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
Thou shall seek them, and shall not find them, even those who contend with thee. Those who war against thee shall be as nothing, and as a thing of naught.
13 Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
For I, Jehovah thy God, will hold thy right hand, saying to thee, Fear not, I will help thee.
14 Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
Fear not, thou worm Jacob, and ye men of Israel. I will help thee, says Jehovah, and thy Redeemer is the Holy One of Israel.
15 “Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
Behold, I have made thee as a new sharp threshing instrument having teeth. Thou shall thresh the mountains, and beat them small, and shall make the hills as chaff.
16 Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
Thou shall winnow them, and the wind shall carry them away, and the whirlwind shall scatter them. And thou shall rejoice in Jehovah. Thou shall glory in the Holy One of Israel.
17 “Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
The poor and needy seek water, and there is none, and their tongue fails for thirst. I, Jehovah, will answer them. I, the God of Israel, will not forsake them.
18 Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
I will open rivers on the bare heights, and fountains in the midst of the valleys. I will make the wilderness a pool of water, and the dry land springs of water.
19 Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
I will put in the wilderness the cedar, the acacia, and the myrtle, and the oil tree. I will set in the desert the fir tree, the pine, and the box tree together,
20 kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
that they may see, and know, and consider, and understand together, that the hand of Jehovah has done this, and the Holy One of Israel has created it.
21 “Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
Produce your case, says Jehovah. Bring forth your strong reasons, says the King of Jacob.
22 Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
Let them bring forth, and declare to us what shall happen. Declare ye the former things, what they are, that we may consider them, and know the latter end of them, or show us things to come.
23 tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
Declare the things that are to come hereafter, that we may know that ye are gods. Yea, do good, or do evil, that we may be dismayed, and behold it together.
24 Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
Behold, ye are of nothing, and your work is of naught. An abomination is he who chooses you.
25 “Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
I have raised up him from the north, and he has come, him who calls upon my name from the rising of the sun. And he shall come upon rulers as upon mortar, and as the potter treads clay.
26 Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
Who has declared it from the beginning, that we may know, and beforetime, that we may say, He is right? Yea, there is none who declares. Yea, there is none who shows. Yea, there is none who hears your words.
27 Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
First to Zion. Behold, behold them, and I will give to Jerusalem him who brings good news.
28 Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
And when I look, there is no man. Even among them there is no counselor, that, when I ask of them, can answer a word.
29 Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.
Behold, all of them, their works are vanity and nothing. Their molten images are wind and confusion.

< Yesaya 41 >