< Yesaya 44 >

1 Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
Yet now hear, O Jacob my servant, and Israel, whom I have chosen.
2 Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
Thus says Jehovah who made thee, and formed thee from the womb, who will help thee: Fear not, O Jacob my servant, and thou, Jeshurun, whom I have chosen.
3 Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
For I will pour water upon him who is thirsty, and streams upon the dry ground. I will pour my Spirit upon thy seed, and my blessing upon thine offspring.
4 Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
And they shall spring up among the grass, as willows by the watercourses.
5 Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
One shall say, I am Jehovah's, and another shall call himself by the name of Jacob, and another shall subscribe with his hand to Jehovah, and surname himself by the name of Israel.
6 “Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
Thus says Jehovah, the King of Israel, and his Redeemer, Jehovah of hosts: I am the first, and I am the last, and besides me there is no God.
7 Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
And who, as I, shall call, and shall declare it, and set it in order for me, since I established the ancient people? And let them declare the things that are coming, and that shall come to pass.
8 Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
Fear ye not, nor be afraid. Have I not declared to thee of old, and shown it? And ye are my witnesses. Is there a God besides me? Yea, there is no Rock. I know not any.
9 Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
Those who fashion a graven image are all of them vanity. And the things that they delight in shall not profit. And their own witnesses see not, nor know, that they may be put to shame.
10 Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
Who has fashioned a god, or molded an image that is profitable for nothing?
11 Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
Behold, all his fellows shall be put to shame, and the workmen. They are of men. Let them all be gathered together. Let them stand up. They shall fear. They shall be put to shame together.
12 Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
The smith makes an axe, and works in the coals, and fashions it with hammers, and works it with his strong arm. Yea, he is hungry, and his strength fails. He drinks no water, and is faint.
13 Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
The carpenter stretches out a line. He marks it out with a pencil. He shapes it with planes. And he marks it out with the compasses, and shapes it after the figure of a man, according to the beauty of a man, to dwell in a house.
14 Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
He hews down cedars for him, and takes the holm tree and the oak, and strengthens for himself one among the trees of the forest. He plants a fir tree, and the rain nourishes it.
15 Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
Then it shall be for a man to burn. And he takes of it, and warms himself. Yea, he kindles it, and bakes bread. Yea, he makes a god, and worships it. He makes it a graven image, and falls down to it.
16 Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
He burns part of it in the fire. With part of it he eats flesh. He roasts roast, and is satisfied. Yea, he warms himself, and says, Aha, I am warm, I have seen the fire.
17 Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
And the residue of it he makes a god, even his graven image. He falls down to it and worships, and prays to it, and says, Deliver me, for thou are my god.
18 Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
They do not know, nor do they consider. For he has shut their eyes, that they cannot see, and their hearts, that they cannot understand.
19 Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
And none calls to mind, nor is there knowledge nor understanding to say, I have burned part of it in the fire. Yea, I have also baked bread upon the coals of it. I have roasted flesh and eaten it. And shall I make the residue of it an abomination? Shall I fall down to the stock of a tree?
20 Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
He feeds on ashes. A deceived heart has turned him aside. And he cannot deliver his soul, nor say, Is there not a lie in my right hand?
21 Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
Remember these things, O Jacob, and Israel, for thou are my servant. I have formed thee. Thou are my servant, O Israel, thou shall not be forgotten by me.
22 Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
I have blotted out, as a thick cloud, thy transgressions, and, as a cloud, thy sins. Return to me, for I have redeemed thee.
23 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
Sing, O ye heavens, for Jehovah has done it. Shout, ye lower parts of the earth. Break forth into singing, ye mountains, O forest, and every tree therein. For Jehovah has redeemed Jacob, and will glorify himself in Israel.
24 Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
Thus says Jehovah, thy Redeemer, and he who formed thee from the womb: I am Jehovah, who makes all things, who stretches forth the heavens alone, who spreads abroad the earth (who is with me?),
25 Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
who frustrates the signs of the liars, and makes diviners mad, who turns wise men backward, and makes their knowledge foolish,
26 Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
who confirms the word of his servant, and performs the counsel of his messengers, who says of Jerusalem, She shall be inhabited, and of the cities of Judah, They shall be built, and I will raise up the waste places of it,
27 Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
who says to the deep, Be dry, and I will dry up thy rivers,
28 Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”
who says of Cyrus, He is my shepherd, and shall perform all my pleasure, even saying of Jerusalem, She shall be built, and of the temple, Thy foundation shall be laid.

< Yesaya 44 >