< Deuteronomo 24 >

1 Ngati mwamuna wakwatira mkazi amene sakukondwera naye chifukwa wapeza vuto pa mkaziyo, namulembera mkaziyo kalata ya chisudzulo, namupatsa ndi kumutulutsa mʼnyumba mwake,
When a man takes a wife, and marries her, then it shall be, if she finds no favor in his eyes, because he has found some unseemly thing in her, that he shall write her a bill of divorcement, and give it in her hand, and send her out of his house.
2 mkaziyo ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina,
And when she has departed out of his house, she may go and be another man's.
3 ndipo mwamuna wachiwiriyo nʼkuyipidwa nayenso ndi kumulemberanso kalata ya chisudzulo nʼkumutulutsa mʼnyumba mwake, kapena ngati mwamunayo amwalira,
And if the latter husband dislikes her, and writes her a bill of divorcement, and gives it in her hand, and sends her out of his house, or if the latter husband dies, who took her to be his wife,
4 mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu.
her former husband, who sent her away, may not take her again to be his wife after she is defiled. For that is abomination before Jehovah, and thou shall not cause the land to sin, which Jehovah thy God gives thee for an inheritance.
5 Mwamuna akangokwatira kumene asamatumizidwe ku nkhondo kapena kupatsidwa ntchito ina iliyonse. Kwa chaka chathunthu akhale ndi ufulu wokhala pa khomo pake kumasangalatsa mkazi wakeyo.
When a man takes a new wife, he shall not go out in the army, neither shall he be charged with any business. He shall be free at home one year, and shall cheer his wife whom he has taken.
6 Munthu akakhala nanu ndi ngongole musamutengere mwala wake wa mphero ngati chikole, chifukwa kutero nʼkumutengera moyo kukhala chikole cha ngongole.
No man shall take the mill or the upper millstone to pledge, for he takes life to pledge.
7 Ngati munthu agwidwa akuba mʼbale wake wa Chiisraeli namamuzunza ngati kapolo kapena kumugulitsa, wogulitsa mnzakeyo ayenera kuphedwa. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
If a man is found stealing any of his brothers of the sons of Israel, and he deals with him harshly, or sells him, then that thief shall die. So shall thou put away the evil from the midst of thee.
8 Pakagwa matenda a khate, samalitsani kuchita zonse zimene ansembe, amene ndi Alevi, anakulangizani. Mutsatire mosamalitsa zimene ndinawalamula.
Take heed in the disease of leprosy, that thou observe diligently, and do according to all that the priests the Levites shall teach you. As I commanded them, so ye shall observe to do.
9 Kumbukirani zimene Yehova Mulungu wanu anachita kwa Miriamu muli paulendo mutatuluka mu Igupto.
Remember what Jehovah thy God did to Miriam by the way as ye came forth out of Egypt.
10 Ukabwereketsa mnzako kanthu kena kalikonse, usalowe mʼnyumba mwake kukatenga chimene wachipereka ngati chikole.
When thou do lend thy neighbor any manner of loan, thou shall not go into his house to fetch his pledge.
11 Uziyima kunja kwa nyumba kuti munthu amene wamubwereketsa kanthuyo akubweretsere kunja komweko.
Thou shall stand outside, and the man to whom thou lend shall bring forth the pledge outside to thee.
12 Ngati munthuyo ndi wosauka, usamutengere chikolecho mpaka kukagona nacho kwanu.
And if he is a poor man, thou shall not sleep with his pledge.
13 Pomalowa dzuwa ukhale utamubwezera mkanjo wakewo kuti akafunde. Pamenepo adzakuthokoza, ndipo amenewa adzawerengedwa ngati machitidwe olungama kwa iweyo pamaso pa Yehova Mulungu wako.
Thou shall surely restore to him the pledge when the sun goes down, that he may sleep in his garment, and bless thee. And it shall be righteousness to thee before Jehovah thy God.
14 Osamapezera mwayi pa anthu aganyu osauka ndi aumphawi, kaya ndi Mwisraeli kapena mlendo wokhala mu umodzi mwa mizinda yanu.
Thou shall not oppress a hired servant who is poor and needy, whether he be of thy brothers, or of thy sojourners that are in thy land within thy gates.
15 Mumulipire malipiro ake a tsiku dzuwa lisanalowe chifukwa ndi wosauka ndipo akudalira malipirowo. Kupanda kutero adzakudandaulirani kwa Yehova ndipo mudzapezeka ochimwa.
Thou shall give him his hire in his day, neither shall the sun go down upon it, for he is poor, and sets his heart upon it, lest he cry against thee to Jehovah, and it be sin to thee.
16 Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.
The fathers shall not be put to death for the sons, neither shall the sons be put to death for the fathers. Every man shall be put to death for his own sin.
17 Musachitire mlendo kapena mwana wamasiye zoyipa, kapena kulanda mkazi wamasiye chovala ngati chikole cha ngongole.
Thou shall not distort the justice due to the sojourner, or to the fatherless, nor take the widow's raiment to pledge,
18 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
but thou shall remember that thou were a bondman in Egypt, and Jehovah thy God redeemed thee from there. Therefore I command thee to do this thing.
19 Mukamakolola mʼmunda mwanu ndipo zokolola zina zikasiyidwa, musamabwerere kukazitola. Muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochita zanu zonse.
When thou reap thy harvest in thy field, and have forgotten a sheaf in the field, thou shall not go again to fetch it. It shall be for the sojourner, for the fatherless, and for the widow, that Jehovah thy God may bless thee in all the work of thy hands.
20 Mukathyola zipatso mu mtengo wa olivi, musamabwererenso kachiwiri ku mtengo womwewo. Zotsalazo zilekereni alendo, ana ndi akazi amasiye.
When thou beat thine olive tree, thou shall not go over the boughs again. It shall be for the sojourner, for the fatherless, and for the widow.
21 Mukakolola mphesa mʼmunda mwanu musamabwereremonso kachiwiri. Zotsalazo muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye.
When thou gather of thy vineyard, thou shall not glean it behind thee. It shall be for the sojourner, for the fatherless, and for the widow.
22 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
And thou shall remember that thou were a bondman in the land of Egypt. Therefore I command thee to do this thing.

< Deuteronomo 24 >