< Deuteronomo 25 >

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
If there be a controversy between men, and they come to judgment, and they judge them, then they shall justify the righteous, and condemn the iniquitous.
2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
And it shall be, if the iniquitous man is deserving to be beaten, that the judge shall cause him to lie down, and to be beaten before his face, according to his iniquity, by number.
3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
He may give him forty stripes. He shall not exceed, lest, if he should exceed, and beat him above these with many stripes, then thy brother should seem debased to thee.
4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
Thou shall not muzzle the ox when he treads out the grain.
5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
If brothers dwell together, and one of them dies, and has no son, the wife of the dead man shall not be married outside to a stranger. Her husband's brother shall go in to her, and take her to him to wife, and perform the duty of a husband's brother to her.
6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
And it shall be, that the firstborn who she bears shall succeed in the name of his brother who is dead, that his name be not blotted out of Israel.
7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
And if the man does not want to take his brother's wife, then his brother's wife shall go up to the gate to the elders, and say, My husband's brother refuses to raise up to his brother a name in Israel. He will not perform the duty of a husband's brother to me.
8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
Then the elders of his city shall call him, and speak to him. And if he stands, and says, I do not want to take her,
9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
then his brother's wife shall come to him in the presence of the elders, and loose his shoe from off his foot, and spit in his face. And she shall answer and say, So shall it be done to the man who does not build up his brother's house.
10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
And his name shall be called in Israel, The house of him who has his shoe loosed.
11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
When men strive together one with another, and the wife of the one draws near to deliver her husband out of the hand of him who smites him, and puts forth her hand, and takes him by the privates,
12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
then thou shall cut off her hand. Thine eye shall have no pity.
13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
Thou shall not have in thy bag diverse weights, a great and a small.
14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
Thou shall not have in thy house diverse measures, a great and a small.
15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
A perfect and just weight thou shall have, a perfect and just measure thou shall have, that thy days may be long in the land which Jehovah thy God gives thee.
16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
For all who do such things, even all who do unrighteously, are an abomination to Jehovah thy God.
17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
Remember what Amalek did to thee by the way as ye came forth out of Egypt,
18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
how he met thee by the way, and smote the hindmost of thee, all who were feeble behind thee, when thou were faint and weary, and he feared not God.
19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!
Therefore it shall be, when Jehovah thy God has given thee rest from all thine enemies round about, in the land which Jehovah thy God gives thee for an inheritance to possess it, that thou shall blot out the remembrance of Amalek from under heaven. Thou shall not forget.

< Deuteronomo 25 >