< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
Now it came to pass after the death of Moses the servant of Jehovah, that Jehovah spoke to Joshua the son of Nun, Moses' minister, saying,
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Moses my servant is dead. Now therefore arise, go over this Jordan, thou, and all this people, to the land which I give to them, even to the sons of Israel.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Every place that the sole of your foot shall tread upon, to you I have given it, as I spoke to Moses.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
From the wilderness, and this Lebanon, even to the great river, the river Euphrates, all the land of the Hittites, and to the great sea toward the going down of the sun, shall be your border.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
There shall not any man be able to stand before thee all the days of thy life. As I was with Moses, so I will be with thee. I will not fail thee, nor forsake thee.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Be strong and of good courage, for thou shall cause this people to inherit the land which I swore to their fathers to give them.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Only be strong and very courageous to observe to do according to all the law, which Moses my servant commanded thee. Turn not from it to the right hand or to the left, that thou may have good success wherever thou go.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
This book of the law shall not depart out of thy mouth, but thou shall meditate on it day and night, that thou may observe to do according to all that is written in it, for then thou shall make thy way prosperous, and then thou shall have good success.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Have I not commanded thee? Be strong and of good courage. Be not frightened, neither be thou dismayed, for Jehovah thy God is with thee wherever thou go.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
Then Joshua commanded the officers of the people, saying,
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Pass through the midst of the camp, and command the people, saying, Prepare food for you, for within three days ye are to pass over this Jordan to go in to possess the land, which Jehovah your God gives you to possess it.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
And to the Reubenites, and to the Gadites, and to the half-tribe of Manasseh, Joshua spoke, saying,
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Remember the word which Moses the servant of Jehovah commanded you, saying, Jehovah your God gives you rest, and will give you this land.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Your wives, your little ones, and your cattle, shall abide in the land which Moses gave you beyond the Jordan, but ye shall pass over before your brothers armed, all the mighty men of valor, and shall help them
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
until Jehovah has given your brothers rest, as you, and they also have possessed the land which Jehovah your God gives them. Then ye shall return to the land of your possession, and possess it, which Moses the servant of Jehovah gave you beyond the Jordan toward the sunrise.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
And they answered Joshua, saying, All that thou have commanded us we will do, and wherever thou send us we will go.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
According as we hearkened to Moses in all things, so will we hearken to thee. Only Jehovah thy God be with thee, as he was with Moses.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Whoever he is who shall rebel against thy commandment, and shall not hearken to thy words in all that thou command him, he shall be put to death. Only be strong and of good courage.

< Yoswa 1 >