< Yoswa 2 >

1 Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
And Joshua the son of Nun sent out of Shittim two men as spies secretly, saying, Go, view the land, and Jericho. And they went and came into the house of a harlot whose name was Rahab, and lay down there.
2 Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
And it was told the king of Jericho, saying, Behold, men came in here tonight of the sons of Israel to search out the land.
3 Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
And the king of Jericho sent to Rahab, saying, Bring forth the men who came to thee, who have entered into thy house, for they have come to search out all the land.
4 Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
And the woman took the two men, and hid them. And she said, Yes, the men came to me, but I did not know from where they were.
5 Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
And it came to pass about the time of the shutting of the gate, when it was dark, that the men went out. Where the men went I know not. Pursue after them quickly, for ye will overtake them.
6 Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
But she had brought them up to the roof, and hid them with the stalks of flax, which she had laid in order upon the roof.
7 Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
And the men pursued after them the way to the Jordan to the fords, and as soon as those who pursued after them were gone out, they shut the gate.
8 Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
And before they were laid down, she came up to them upon the roof.
9 ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
And she said to the men, I know that Jehovah has given you the land, and that the fear of you has fallen upon us. And that all the inhabitants of the land melt away before you.
10 Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
For we have heard how Jehovah dried up the water of the Red Sea before you when ye came out of Egypt, and what ye did to the two kings of the Amorites who were beyond the Jordan, to Sihon and to Og, whom ye utterly destroyed.
11 Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
And as soon as we had heard it, our hearts melted, neither did there remain any more spirit in any man because of you, for Jehovah your God, he is God in heaven above, and on earth beneath.
12 Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
Now therefore, I pray you, swear to me by Jehovah, since I have dealt kindly with you, that ye also will deal kindly with my father's house, and give me a true token,
13 Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
and that ye will save alive my father, and my mother, and my brothers, and my sisters, and all that they have, and will deliver our lives from death.
14 Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
And the men said to her, Our life for yours if ye do not utter this our business. And it shall be, when Jehovah gives us the land, that we will deal kindly and truly with thee.
15 Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
Then she let them down by a cord through the window, for her house was upon the side of the wall, and she dwelt upon the wall.
16 Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
And she said to them, Get you to the mountain lest the pursuers come upon you. And hide yourselves there three days, until the pursuers be returned, and afterward ye may go your way.
17 Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
And the men said to her, We will be guiltless of this thine oath which thou have made us to swear.
18 tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
Behold, when we come into the land, thou shall bind this line of scarlet cord in the window which thou let us down by. And thou shall gather to thee into the house thy father, and thy mother, and thy brothers, and all thy father's household.
19 Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
And it shall be, that whoever shall go out of the doors of thy house into the street, his blood shall be upon his head, and we shall be guiltless. And whoever shall be with thee in the house, his blood shall be on our head if any hand be upon him.
20 Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
But if thou utter this our business, then we shall be guiltless of thine oath which thou have made us to swear.
21 Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
And she said, According to your words, so be it. And she sent them away, and they departed. And she bound the scarlet line in the window.
22 Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
And they went, and came to the mountain, and abode there three days, until the pursuers were returned. And the pursuers sought them throughout all the way, but did not find them.
23 Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
Then the two men returned, and descended from the mountain, and passed over, and came to Joshua the son of Nun. And they told him all that had befallen them.
24 Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”
And they said to Joshua, Truly Jehovah has delivered into our hands all the land, and moreover all the inhabitants of the land melt away before us.

< Yoswa 2 >