< Deuteronomo 34 >

1 Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.
And Moses went up from the plains of Moab to mount Nebo, to the top of Pisgah, that is opposite Jericho. And Jehovah showed him all the land of Gilead, to Dan,
2 Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja,
and all Naphtali, and the land of Ephraim and Manasseh, and all the land of Judah, to the farther sea,
3 Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari.
and the South, and the Plain of the valley of Jericho the city of palm trees, to Zoar.
4 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
And Jehovah said to him, This is the land which I swore to Abraham, to Isaac, and to Jacob, saying, I will give it to thy seed. I have caused thee to see it with thine eyes, but thou shall not go over there.
5 Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova.
So Moses the servant of Jehovah died there in the land of Moab, according to the word of Jehovah.
6 Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake.
And he buried him in the valley in the land of Moab opposite Beth-peor, but no man knows of his sepulcher to this day.
7 Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu.
And Moses was a hundred and twenty years old when he died. His eye was not dim, nor his natural force abated.
8 Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
And the sons of Israel wept for Moses in the plains of Moab thirty days. So the days of weeping and mourning for Moses were ended.
9 Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
And Joshua the son of Nun was full of the spirit of wisdom, for Moses had laid his hands upon him. And the sons of Israel hearkened to him, and did as Jehovah commanded Moses.
10 Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso.
And there has not arisen a prophet since in Israel like Moses, whom Jehovah knew face to face,
11 Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse.
in all the signs and the wonders, which Jehovah sent him to do in the land of Egypt, to Pharaoh, and to all his servants, and to all his land,
12 Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.
and in all the mighty hand, and in all the great terror, which Moses wrought in the sight of all Israel.

< Deuteronomo 34 >