< Deuteronomo 26 >

1 Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
And it shall be, when thou have come in to the land which Jehovah thy God gives thee for an inheritance, and possess it, and dwell in it,
2 mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
that thou shall take of the first of all the fruit of the ground, which thou shall bring in from thy land that Jehovah thy God gives thee, and thou shall put it in a basket, and shall go to the place which Jehovah thy God shall choose to cause his name to dwell there.
3 ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
And thou shall come to the priest who shall be in those days, and say to him, I profess this day to Jehovah thy God, that I have come to the land which Jehovah swore to our fathers to give us.
4 Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
And the priest shall take the basket out of thy hand, and set it down before the altar of Jehovah thy God.
5 Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
And thou shall answer and say before Jehovah thy God, My father was a Syrian ready to perish, and he went down into Egypt, and sojourned there, few in number. And he became there a nation, great, mighty, and populous.
6 Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
And the Egyptians dealt ill with us, and afflicted us, and laid upon us hard bondage.
7 Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
And we cried to Jehovah, the God of our fathers, and Jehovah heard our voice, and saw our affliction, and our toil, and our oppression.
8 Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
And Jehovah brought us forth out of Egypt with a mighty hand, and with an outstretched arm, and with great terribleness, and with signs, and with wonders.
9 Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
And he has brought us into this place, and has given us this land, a land flowing with milk and honey.
10 Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
And now, behold, I have brought the first of the fruit of the ground, which thou, O Jehovah, have given me. And thou shall set it down before Jehovah thy God, and worship before Jehovah thy God.
11 Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
And thou shall rejoice in all the good which Jehovah thy God has given to thee, and to thy house, thou, and the Levite, and the sojourner who is in the midst of thee.
12 Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
When thou have made an end of tithing all the tithe of thine increase in the third year, which is the year of tithing, then thou shall give it to the Levite, to the sojourner, to the fatherless, and to the widow, that they may eat within thy gates, and be filled.
13 Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
And thou shall say before Jehovah thy God, I have put away the hallowed things out of my house, and also have given them to the Levite, and to the sojourner, to the fatherless, and to the widow, according to all thy commandment which thou have commanded me. I have not transgressed any of thy commandments, neither have I forgotten them.
14 Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
I have not eaten of it in my mourning, neither have I put away from it, being unclean, nor given of it for the dead. I have hearkened to the voice of Jehovah my God. I have done according to all that thou have commanded me.
15 Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
Look down from thy holy habitation, from heaven, and bless thy people Israel, and the ground which thou have given us, as thou swore to our fathers, a land flowing with milk and honey.
16 Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
This day Jehovah thy God commands thee to do these statutes and ordinances. Thou shall therefore keep and do them with all thy heart, and with all thy soul.
17 Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
Thou have avouched Jehovah this day to be thy God, and that thou would walk in his ways, and keep his statutes, and his commandments, and his ordinances, and hearken to his voice.
18 Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
And Jehovah has avouched thee this day to be a people for his own possession, as he has promised thee, and that thou should keep all his commandments,
19 Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.
and to make thee high above all nations that he has made, in praise, and in name, and in honor, and that thou may be a holy people to Jehovah thy God, as he has spoken.

< Deuteronomo 26 >