< Deuteronomo 22 >

1 Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye.
Thou shall not see thy brother's ox or his sheep go astray, and hide thyself from them. Thou shall surely bring them again to thy brother.
2 Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere.
And if thy brother be not near to thee, or if thou do not know him, then thou shall bring it home to thy house, and it shall be with thee until thy brother seeks after it, and thou shall restore it to him.
3 Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.
And so shall thou do with his donkey, and so shall thou do with his garment, and so shall thou do with every lost thing of thy brother's, which he has lost, and thou have found. Thou may not hide thyself.
4 Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.
Thou shall not see thy brother's donkey or his ox fallen down by the way, and hide thyself from them. Thou shall surely help him to lift them up again.
5 Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.
A woman shall not wear that which pertains to a man, neither shall a man put on a woman's garment, for whoever does these things is an abomination to Jehovah thy God.
6 Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe.
If a bird's nest chance to be before thee in the way, in any tree or on the ground, with young ones or eggs, and the dam sitting upon the young or upon the eggs, thou shall not take the dam with the young.
7 Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.
Thou shall surely let the dam go, but the young thou may take to thyself, that it may be well with thee, and that thou may prolong thy days.
8 Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.
When thou build a new house, then thou shall make a guard rail for thy roof, that thou not bring blood upon thy house, if any man falls from there.
9 Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.
Thou shall not sow thy vineyard with two kinds of seed, lest the whole fruit be forfeited: the seed which thou have sown, and the increase of the vineyard.
10 Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.
Thou shall not plow with an ox and a donkey together.
11 Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.
Thou shall not wear a mingled stuff, wool and linen together.
12 Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.
Thou shall make for thee hems upon the four borders of thy clothing, with which thou cover thyself.
13 Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso
If any man takes a wife, and goes in to her, and dislikes her,
14 namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,”
and charges her with shameful things, and brings up an evil name upon her, and says, I took this woman, and when I came near to her, I did not find in her the tokens of virginity,
15 zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata.
then the father of the damsel, and her mother, shall take and bring forth the tokens of the damsel's virginity to the elders of the city in the gate.
16 Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso.
And the damsel's father shall say to the elders, I gave my daughter to this man to wife, and he dislikes her.
17 Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja,
And, lo, he has charged her with shameful things, saying, I did not find in thy daughter the tokens of virginity, and yet these are the tokens of my daughter's virginity. And they shall spread the garment before the elders of the city.
18 ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango.
And the elders of that city shall take the man and chastise him,
19 Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.
and they shall fine him a hundred shekels of silver, and give them to the father of the damsel, because he has brought up an evil name upon a virgin of Israel, and she shall be his wife. He may not put her away all his days.
20 Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke,
But if this thing be true, that the tokens of virginity were not found in the damsel,
21 iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.
then they shall bring the damsel out to the door of her father's house, and the men of her city shall stone her to death with stones, because she has wrought folly in Israel, to play the harlot in her father's house. So shall thou put away the evil from the midst of thee.
22 Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.
If a man be found lying with a woman married to a husband, then they shall both of them die, the man that lay with the woman, and the woman. So shall thou put away the evil from Israel.
23 Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye,
If there be a damsel who is a virgin betrothed to a husband, and a man finds her in the city, and lies with her,
24 muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
then ye shall bring them both out to the gate of that city. And ye shall stone them to death with stones, the damsel, because she did not cry out, being in the city, and the man, because he has humbled his neighbor's wife. So thou shall put away the evil from the midst of thee.
25 Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa.
But if the man finds the damsel who is betrothed in the field, and the man forces her, and lies with her, then only the man who lay with her shall die,
26 Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye,
but to the damsel thou shall do nothing. There is in the damsel no sin worthy of death. For as when a man rises against his neighbor, and kills him, even so is this matter,
27 pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.
for he found her in the field, the betrothed damsel cried out, and there was none to save her.
28 Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka,
If a man finds a damsel who is a virgin, who is not betrothed, and lays hold on her, and lies with her, and they be found,
29 ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.
then the man who lay with her shall give to the damsel's father fifty shekels of silver, and she shall be his wife, because he has humbled her. He may not put her away all his days.
30 Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.
A man shall not take his father's wife, and shall not uncover his father's skirt.

< Deuteronomo 22 >