< Deuteronomo 33 >

1 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe.
This is the blessing, bi which Moises, the man of God, blesside the sones of Israel bifor his deeth;
2 Iye anati: “Yehova anabwera kuchokera ku Sinai ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri; anawala kuchokera pa Phiri la Parani. Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
and seide, The Lord cam fro Syna, and he roos to us fro Seir; he apperide fro the hil of Pharan, and thousandis of seyntis with hym; a lawe of fier in his riythond.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu; opatulika ake onse ali mʼmanja mwake. Onse amagwada pansi pa mapazi anu kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
He louede puplis; alle seyntis ben in his hond, and thei that neiyen to hise feet schulen take of his doctryn.
4 malamulo amene Mose anatipatsa, chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
Moisis comaundide lawe `to vs, eritage of the multitude of Jacob.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, pamodzi ndi mafuko a Israeli.
And the king schal be at the moost riytful, whanne princes of the puple schulen be gaderid togidere with the lynagis of Israel.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe, anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
Ruben lyue, and die not, and be he litil in noumbre.
7 Ndipo ponena za Yuda anati: “Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda; mubweretseni kwa anthu ake. Ndi manja ake omwe adziteteze yekha. Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
This is the blessyng of Juda; Lord, here thou the vois of Juda, and brynge in hym to his puple; hise hondis schulen fiyte for hym, and the helpere of hym schal be ayens hise aduersaries.
8 Za fuko la Alevi anati: “Tumimu wanu ndi Urimu ndi za mtumiki wanu wokhulupirika. Munamuyesa ku Masa; munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
Also he seide to Leuy, Thi perfeccioun and thi techyng is of an hooly man, whom thou preuedist in temptacioun, and demedist at the Watris of Ayenseiynge;
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti, ‘Sindilabadira za iwo.’ Sanasamale za abale ake kapena ana ake, koma anayangʼanira mawu anu ndipo anateteza pangano lanu.
which Leuy seide to his fadir and to his modir, Y knowe not you, and to hise britheren, Y knowe not hem; and knewen not her sones. These kepten thi speche, and these kepten thi couenaunt; A!
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu ndi malamulo anu kwa Israeli. Amafukiza lubani pamaso panu ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
Jacob, thei kepten thi domes, and `thou, Israel, thei kepten thi lawe; thei schulen putte encense in thi strong veniaunce, and brent sacrifice on thin auter.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake. Menyani adani awo mʼchiwuno kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
Lord, blesse thou the strengthe of hym, and resseyue thou the werkis of his hondis; smyte thou the backis of hise enemyes, and thei that haten hym, rise not.
12 Za fuko la Benjamini anati: “Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye, pakuti amamuteteza tsiku lonse, ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
And he seide to Benjamyn, The moost loued of the Lord schal dwelle tristili in hym, `that is, in the Lord; he schal dwelle al day as in a chaumbur, and he schal reste bitwixe the schuldris of hym.
13 Za fuko la Yosefe anati: “Yehova adalitse dziko lake ndi mame ambiri ochokera kumwamba ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
Also he seide to Joseph, `His lond is of the Lordis blessyng; of the applis of heuene, and of the dewe, and of watir liggynge bynethe;
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
of the applis of fruytis of the sunne and moone; of the coppe of elde munteyns,
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
and of the applis of euerlastynge litle hillis;
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto. Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe, wapaderadera pakati pa abale ake.
and of the fruytis of the lond, and of the fulnesse therof. The blessyng of hym that apperide in the busch come on the heed of Joseph, and on the cop of Nazarey, `that is, hooli, among hise britheren.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa; nyanga zake zili ngati za njati. Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina, ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi. Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu; nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
As the first gendrid of a bole is the feirnesse of hym; the hornes of an vnicorn ben the hornes of hym; in tho he schal wyndewe folkis, `til to the termes of erthe. These ben the multitudis of Effraym, and these ben the thousyndis of Manasses.
18 Za fuko la Zebuloni anati: “Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka, ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
And he seide to Zabulon, Zabulon, be thou glad in thi goyng out, and, Ysacar, in thi tabernaclis.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri, kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo; kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja, chuma chobisika mu mchenga.”
Thei schulen clepe puplis to the hil, there thei schulen offre sacrifices of riytfulnesse; whiche schulen souke the flowing of the see as mylk, and hid tresours of grauel.
20 Za fuko la Gadi anati: “Wodala amene amakulitsa malire a Gadi! Gadi amakhala kumeneko ngati mkango, kukhadzula mkono kapena mutu.
And he seide to Gad, Gad is blessid in broodnesse; he restide as a lioun, and he took the arm and the nol.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri; gawo la mtsogoleri anasungira iye. Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, anachita chifuniro cha Yehova molungama, ndiponso malamulo onena za Israeli.”
And he siy his prinshed, that `the techere was kept in his part; which Gad was with the princes of the puple, and dide the riytfulnesses of the Lord, and his doom with Israel.
22 Za fuko la Dani anati: “Dani ndi mwana wamkango, amene akutuluka ku Basani.”
Also he seide to Dan, Dan, a whelp of a lioun, schal flowe largeli fro Basan.
23 Za fuko la Nafutali anati: “Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake; cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
And he seide to Neptalym, Neptalym schal vse abundaunce, and he schal be ful with blessyngis of the Lord; and he schal welde the see and the south.
24 Za fuko la Aseri anati: “Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri; abale ake amukomere mtima, ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
Also he seide to Aser, Aser, be blessid in sones, and plese he hise britheren; dippe he his foot in oile.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa, ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
Yrun and bras the scho of hym; as the dai of thi youthe so and thin eelde.
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni, amene amakwera pa thambo kukuthandizani ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
Noon other god is as the God of the moost riytful, that is, `as the God `of the puple of Israel, gouerned bi moost riytful lawe; the stiere of heuene is thin helpere; cloudis rennen aboute bi the glorie of hym.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu, ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha. Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu, adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
His dwellynge place is aboue, and armes euerlastynge ben bynethe; he schal caste out fro thi face the enemy, and he schal seie, Be thou al to-brokun.
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere; zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano, kumene thambo limagwetsa mame.
Israel schal dwelle trustili and aloone; the iye of Jacob in the lond of whete, and of wyn; and heuenes schulen be derk with dew.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala! Wofanana nanu ndani anthu opulumutsidwa ndi Yehova? Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu ndi lupanga lanu la ulemerero. Adani ako adzakugonjera, ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Blessed art thou, Israel; thou puple that art saued in the Lord, who is lijk thee? The scheld of thin help and the swerd of thi glorie is thi God; thin enemyes schulen denye thee, and thou schalt trede her neckis.

< Deuteronomo 33 >