< Deuteronomo 34 >

1 Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.
Therfor Moyses stiede fro the feeldi places of Moab on the hil of Nebo, in to the cop of Fasga, ayens Gerico. And the Lord schewide to hym al the lond of Galaad `til to Dan,
2 Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja,
and al Neptalym, and the lond of Effraym and of Manasses, and al the lond of Juda, `til to the laste see; and the south part,
3 Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari.
and the breede of the feeld of Jerico, of the citee of Palmes `til to Segor.
4 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
And the Lord seide to hym, This is the lond for which Y swoor to Abraham, Isaac, and Jacob; and Y seide, Y schal yyue it to thi seed; thou hast seyn it with thin iyen, and thou schalt not passe `to it.
5 Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova.
And Moyses, the seruaunt of the Lord, was deed there, in the lond of Moab, `for the Lord comaundide.
6 Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake.
And the Lord biriede hym in a valey of the lond of Moab, ayens Fegor, and no man knewe his sepulcre `til in to present day.
7 Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu.
Moises was of an hundrid and twenti yeer whanne he diede; his iye dasewide not, nethir hise teeth weren stirid.
8 Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
And the sones of Israel biwepten hym thretti daies in the feeldi places of Moab; and the daies of weilyng of men `bymorenynge Moises weren fillid.
9 Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
Forsothe Josue, the sone of Nun, was fillid with `the spyrit of wisdom, for Moises settide hise hondis on hym; and the sones of Israel obeieden to Josue, and diden as the Lord comaundide to Moises.
10 Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso.
And `a profete roos no more in Israel `as Moises, whom the Lord knewe face to face,
11 Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse.
in alle myraclis, and grete wondris, whiche the Lord sente bi hym, that he schulde do in the lond of Egipt to Farao, and alle hise seruauntis, and to al the lond `of hym,
12 Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.
and al strong hond, and the `grete merueylis, whiche Moyses dide bifor al Israel.

< Deuteronomo 34 >