< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
And the Lord spak to Moises in the deseert of Synay, in the tabernacle of the boond of pees, in the firste day of the secounde monethe, in the tother yeer of her goyng out of Egipt,
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
and seide, Take ye `the summe of al the congregacioun of the sones of Israel, bi her kynredis, and howsis, and `the names of alle bi hem silf, what
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
euer thing is of male kynde fro the twentithe yeere and aboue, of alle the stronge men of Israel; and thou and Aaron schulen noumbre hem bi her cumpanies.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
And the princes of lynagis and of housis, in her kynredis, schulen be with you,
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
of whiche princes these ben the names; of Ruben, Elisur, the sone of Sedeur;
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
of Symeon, Salamyel, the sone of Suri Sadday;
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
of Juda, Naason, the sone of Amynadab; of Ysacar,
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Nathanael, the sone of Suar;
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
of Zabulon, Eliab, the sone of Elon; sotheli of the sones of Joseph,
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
of Effraym, Elisama, the sone of Amyud; of Manasses, Gamaliel the sone of Phadussur;
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
of Beniamyn, Abidan, the sone of Gedeon;
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
of Dan, Aiezer, the sone of Amysadday;
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
of Aser, Fegiel, the sone of Ochran;
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
of Gad, Elisaphan, the sone of Duel;
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
of Neptalym, Hayra, the sone of Henam.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These weren the noblest princes of the multitude, bi her lynagis, and kynredis, and the heedis of the oost of Israel,
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
whiche pryncis Moises and Aaron token, with al the multitude of the comyn puple.
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
And thei gaderiden in the firste dai of the secounde monethe, and telden hem bi kynredis, and housis, and meynees, and heedis, and names of alle by hem silf, fro the twentithe yeer and aboue,
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
as the Lord comaundide to Moises.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
And of Ruben the firste gendrid of Israel weren noumbrid, in the deseert of Synai, bi her generaciouns, and meynees, and housis, and bi the names of alle heedis, al thing that is of male kynde, fro `the twentithe yeer and aboue, of men goynge forth to batel,
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
sixe and fourti thousynd and fyue hundrid.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Symeon, bi her generaciouns, and meynees, and housis of her kyneredis, weren noumbrid, bi the names and heedis of alle, al that is of male kynde, fro `the twentithe yeer and aboue, of men goynge forth to batel,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
nyn and fifty thousand and thre hundrid.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Gad, by generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro twenti yeer and aboue, alle men that yeden forth to batels,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
fyue and fourti thousand sixe hundrid and fifti.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Juda, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, by the names of alle, fro `the twentithe yeer and aboue, alle men that miyten go to batels,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
weren noumbrid foure and seuenti thousand and sixe hundrid.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Ysacar, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, bi the names of alle, fro `the twentithe yeer and aboue, alle men that yeden forth to batels,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
weren noumbrid foure and fifti thousande and foure hundrid.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Zabulon, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro `the twentithe yeer and aboue, alle men that myyten go forth to batels,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
seuene and fifti thousynde and foure hundrid.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Joseph, of the sones of Effraym, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro `the twentithe yeer and aboue, alle men that myyten go forth to batels,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
fourti thousynde and fyue hundrid.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Forsothe of the sones of Manasses, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro the twentithe yeer and aboue, alle men that myyten go forth to batels,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
two and thretti thousynd and two hundrid.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Beniamyn, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro twenti yeer and aboue, alle men that miyten go forth to batels,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
fyue and thretti thousinde and foure hundrid.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Dan, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro `the twentithe yere and aboue, alle men that myyten go forth to batels,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
two and sixti thousynde and seuene hundrid.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Aser, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro `the twentithe yeer and aboue, alle men that myyten go forth to batels,
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
fourti thousynde and a thousynde and fyue hundrid.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sones of Neptalym, bi generaciouns, and meynees, and housis of her kynredis, weren noumbrid, bi the names of alle, fro `the twentithe yeer and aboue, alle men that myyten go forth to batels,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
thre and fifty thousynde and foure hundrid.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These men it ben, whiche Moises and Aaron and the twelue princes of Israel noumbriden, alle bi the housis `of her kynredis.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
And alle men of the sones of Israel bi her housis, and meynees, fro `the twentithe yeer and aboue, that myyten go forth to batels, weren togidere
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
sixe hundrid thousynde and thre thousynde of men, fyue hundred and fifti.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Sotheli the dekenes in the lynage of her meynes weren not noumbrid with hem.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide, `Nyle thou noumbre the lynage of Leuy,
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
nether sette thou the summe of hem with the sones of Israel;
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
but thou schalt ordeyne hem on the tabernacle of witnessing, and on alle the vessels therof, and what euer thing perteyneth to cerymonyes ether sacrifices. Thei schulen bere the tabernacle, and alle purtenaunces therof, and thei schulen be in seruyce, and schulen sette tentis bi the cumpas of the tabernacle.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Whanne me schal go, the dekenes schulen do doun the tabernacle; whanne the tentis schulen be sette, thei schulen `reise the tabernacle. Who euer of straungeris neiyeth, he schal be slayn.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Sotheli the sones of Israel schulen sette tentis, ech man bi cumpenyes, and gaderyngis, and his oost;
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
forsothe the dekenes schulen sette tentis bi the cumpas of the tabernacle, lest indignacioun be maad on the multitude of the sones of Israel; and thei schulen wake in the kepyngis of the `tabernacle of witnessyng.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Therfor the sones of Israel diden bi alle thingis whiche the Lord comaundide to Moises.

< Numeri 1 >