< Deuteronomo 32 >

1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Ye heuenes, here what thingis Y schal speke; the erthe here the wordis of my mouth.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
My techyng wexe togidere as reyn; my speche flete out as dew, as lytil reyn on eerbe, and as dropis on gras.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
For Y schal inwardli clepe the name of the Lord; yyue ye glorie to oure God.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
The werkis of God ben perfit, and alle hise weies ben domes; God is feithful, and without ony wickidnesse; God is iust and riytful.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
Thei synneden ayens hym, and not hise sones in filthis, `that is, of idolatrie; schrewid and waiward generacioun.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
Whether thou yeldist these thingis to the Lord, thou fonned puple and vnwijs? Whether he is not thi fadir, that weldide thee, and made, `and made thee of nouyt?
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Haue thou minde of elde daies, thenke thou alle generaciouns; axe thi fadir, and he schal telle to thee, axe thi grettere men, and thei schulen seie to thee.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
Whanne the hiyeste departide folkis, whanne he departide the sones of Adam, he ordeynede the termes of puplis bi the noumbre of the sones of Israel.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
Forsothe the part of the Lord is his puple; Jacob is the litil part of his eritage.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
The Lord foond hym in a deseert lond, `that is, priued of Goddis religioun, in the place of orrour `ethir hidousnesse, and of wast wildirnesse; the Lord ledde hym aboute, and tauyte hym, and kepte as the apple of his iye.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
As an egle stirynge his briddis to fle, and fleynge on hem, he spredde forth his wyngis, and took hem, and bar in hise schuldris.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
The Lord aloone was his ledere, and noon alien god was with hym.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
The Lord ordeynede hym on an hiy lond, that he schulde ete the fruytis of feeldis, that he schulde souke hony of a stoon, and oile of the hardeste roche;
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
botere of the droue, and mylke of scheep, with the fatnesse of lambren and of rammes, of the sones of Basan; and that he schulde ete kydis with the merowe of wheete, and schulde drynke the cleereste blood of grape.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
The louede puple was `maad fat, and kikide ayen; maad fat withoutforth, maad fat with ynne, and alargid; he forsook God his makere, and yede awei fro `God his helthe.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
Thei terriden hym to ire in alien goddis, and thei excitiden to wrathfulnesse in abhomynaciouns.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
Thei offriden to feendis, and not to God, to goddis whiche thei knewen not, newe goddis, and freische camen, whiche `the fadris of hem worschipiden not.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
Thou hast forsake God that gendride thee, and thou hast foryete `thi Lord creatour.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
The Lord siy, and was stirid to wrathfulnesse; for hise sones and douytris terriden hym.
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
And the Lord seide, Y schal hyde my face fro hem, and Y schal biholde `the laste thingis of hem; for it is a waiward generacioun, and vnfeithful sones.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
Thei terriden me in hym that was not God, and thei `terriden to ire in her vanytees; and Y schal terre hem in hym, that is not a puple, and Y schal terre hem `to yre in a fonned folk.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
Fier, that is, peyne maad redi to hem, is kyndlid in my stronge veniaunce, and it schal brenne `til to the laste thingis of helle; and it schal deuoure the lond with his fruyt, and it schal brenne the foundementis of hillis. (Sheol h7585)
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
Y schal gadere `yuels on hem, and Y schal fille myn arewis in hem.
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
Thei schulen be waastid with hungur, and briddis schulen deuoure hem with bitteriste bityng; Y schal sende in to hem the teeth of beestis, with the woodnesse of wormes drawynge on erthe, and of serpentis.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
Swerd with outforth and drede with ynne schal waaste hem; a yong man and a virgyn togidre, a soukynge child with an elde man.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
And Y seide, Where ben thei? Y schal make the mynde of hem to ceesse of men.
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
But Y delayede for the yre of enemyes, lest perauenture `the enemyes of hem shulden be proude, and seie, Oure hiy hond, and not the Lord, dide alle these thingis.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
It is a folk with out counsel, and with out prudence;
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
Y wolde that thei saueriden, and `vnderstoden, and purueiden the laste thingis.
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
How pursuede oon of enemyes a thousynde of Jewis, and tweyne dryuen awey ten thousynde? Whether not therfore for her God selde hem, and the Lord closide hem togidere?
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
For oure God is not as the goddis of hem, and oure enemyes ben iugis.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
The vyner of hem is of the vyner of Sodom, and of the subarbis of Gomorre; the grape of hem is the grape of galle, and the clustre is most bittir.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
The galle of dragouns is the wyn of hem, and the venym of eddris, that may not be heelid.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
Whether these thingis ben not hid at me, and ben seelid in myn tresouris?
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
Veniaunce is myn, and Y schal yelde to hem in tyme, that the foot of hem slide; the dai of perdicioun is nyy, and tymes hasten to be present.
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
The Lord schal deme his puple, and he schal do merci in hise seruauntis; the puple schal se that the hond of fiyteres is sijk, and also men closid failiden, and the residues ben waastid.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
And thei schulen seie, Where ben `the goddis of hem, in whiche thei hadden trust?
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
Of whos sacrifices thei eeten fatnessis, and drunkun the wyn of fletynge sacrifices, rise thei and helpe you, and defende thei you in nede.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
Se ye that Y am aloone, and noon other God is outakun me; Y schal sle, and Y schal make to lyue; Y schal smyte, and Y schal make hool; and noon is that may delyuere fro myn hond.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
And Y schal reise myn hond to heuene, and Y schal seie, Y lyue with outen ende.
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
If Y schal whette my swerd as leit, and myn hond schal take doom, Y schal yelde veniaunce to myn enemyes, and Y schal quyte to hem that haten me.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
Y schal fille myn arewis with blood, and my swerd schal deuoure fleischis of the blood of hem that ben slayn, and of the caitifte of the heed of enemyes maad nakid.
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Folkis, preise ye the puplis of hym, for he schal venie the blood of hise seruauntis, and he schal yelde veniaunce in to the enemyes of hem; and he schal be merciful to the lond of his puple.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
Therfor Moises cam, and spak alle the wordis of this song in the eeris of the puple; bothe he and Josue, the sone of Nun.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
And `he fillide alle these wordis, and spak to alle Israel, and seide to hem,
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
Putte ye youre hertis in to alle the wordis whiche Y witnesse to you to day, that ye comaunde to youre sones, to kepe, and do tho, and to fulfille alle thingis that ben writun in the book of this lawe;
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
for not in veyn tho ben comaundid to you, but that alle men schulden lyue in tho; whiche wordis ye schulen do, and schulen contynue in long tyme in the lond, to which ye schulen entre to welde, whanne Jordan is passid.
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises in the same day,
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
and seide, Stie thou in to this hil Abirym, that is, passyng, in to the hil of Nebo, which is in the lond of Moab, ayens Jerico; and se thou the lond of Canaan, which Y schal yyue to the sones of Israel to holde, and die thou in the hil.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
In to which hil thou schalt stie, and schalt be ioyned to thi puplis, as Aaron, thi brother, was deed in the hil of Hor, and was put to his puplis.
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
For ye trespassiden ayens me, in the myddis of the sones of Israel, at the Watris of Ayenseiyng, in Cades of deseert of Syn; and ye halewiden not me among the sones of Israel.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
Ayenward thou schalt se the lond, and schalt not entre in to it, which Y schal yyue to the sones of Israel.

< Deuteronomo 32 >