< 2 Mafumu 24 >

1 Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
Za njegova vremena doðe Navuhodonosor car Vavilonski; i Joakim mu bi sluga tri godine; potom odusta i odmetnu se od njega.
2 Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
I Gospod posla na nj èete Haldejske i èete Sirske i èete Moavske i èete sinova Amonovijeh; posla ih na Judu da ga potru, po rijeèi Gospodnjoj koju govori preko sluga svojih proroka.
3 Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
Po zapovijesti Gospodnjoj zbi se to Judi da bi ga odbacio od sebe za grijehe Manasijine po svemu što bješe uèinio;
4 kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
I za krv pravu koju bješe prolio napunivši Jerusalim krvi prave; zato Gospod ne htje oprostiti.
5 Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A ostala djela Joakimova i sve što je uèinio, nije li zapisano u dnevniku careva Judinijeh?
6 Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Joakim kod otaca svojih; a na njegovo se mjesto zacari Joahin.
7 Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
A car Misirski ne izide više iz zemlje svoje, jer car Vavilonski uze od rijeke Misirske do rijeke Efrata sve što bješe cara Misirskoga.
8 Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
Osamnaest godina bijaše Joahinu kad se zacari, i carova tri mjeseca u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Neusta, kæi Elnatanova, iz Jerusalima.
9 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
I on èinjaše zlo pred Gospodom sasvijem kako je èinio otac njegov.
10 Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
U to vrijeme doðoše sluge Navuhodonosora cara Vavilonskoga na Jerusalim, i grad bi opkoljen.
11 ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
Doðe i Navuhodonosor car Vavilonski na grad kad ga sluge njegove opkoliše.
12 Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
Tada Joahin car Judin izide k caru Vavilonskom s materom svojom i sa slugama svojim i s knezovima svojim i s dvoranima svojim; a car ga Vavilonski zarobi osme godine svojega carovanja.
13 Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
I odnese sve blago doma Gospodnjega i blago doma carskoga, i polupa sve sudove zlatne, koje bješe naèinio Solomun car Izrailjev za crkvu Gospodnju, kao što bješe rekao Gospod.
14 Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
I preseli sav Jerusalim, sve knezove i sve junake, deset tisuæa robova, i sve drvodjelje i sve kovaèe, ne osta ništa osim siromašnoga naroda po zemlji.
15 Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
Odvede i Joahina u Vavilon i mater carevu i žene careve i dvorane njegove, i glavare zemaljske odvede u ropstvo iz Jerusalima u Vavilon.
16 Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
I sve junake, na broj sedam tisuæa, i drvodjelje i kovaèe, tisuæu, sve što bijahu za vojsku odvede car Vavilonski u Vavilon u ropstvo.
17 Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
I postavi carem car Vavilonski na mjesto Joahinovo Mataniju strica njegova, i predje mu ime Sedekija.
18 Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Dvadeset i jedna godina bješe Sedekiji kad poèe carovati, i carova jedanaest godina u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Amutala, kæi Jeremijina, iz Livne.
19 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
On èinjaše što je zlo pred Gospodom sasvijem kako je èinio Joakim.
20 Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.
Jer od gnjeva Gospodnjega zbi se to Jerusalimu i Judi, da ih odbaci od sebe. A Sedekija se odmetnu od cara Vavilonskoga.

< 2 Mafumu 24 >