< 2 Mafumu 23 >

1 Pamenepo mfumu inayitanitsa akuluakulu onse a ku Yuda ndi Yerusalemu.
Tada posla car, te se skupiše k njemu sve starješine Judine i Jerusalimske.
2 Mfumuyo inapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, ndi onse okhala mu Yerusalemu, ansembe ndi aneneri, ndiponso anthu ena onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Mfumuyo inawerenga mawu onse a mʼBuku la Chipangano limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova, anthu onse akumva.
I otide car u dom Gospodnji i s njim svi ljudi iz zemlje Judine i svi Jerusalimljani i sveštenici i proroci i sav narod, malo i veliko, i proèita im sve rijeèi knjige zavjetne, koja se naðe u domu Gospodnjem.
3 Mfumu inayimirira pambali pa chipilala ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova kuti idzatsatira Yehova ndi kusunga malamulo, mawu ndi malangizo ake ndi mtima wonse ndi moyo wonse, kukwaniritsa mawu a mʼpanganoli, olembedwa mʼbukuli. Pamenepo anthu onse anadzipereka kutsatira panganoli.
I car stojeæi kod stupa uèini zavjet pred Gospodom da æe oni iæi za Gospodom i držati zapovijesti njegove i svjedoèanstva njegova i uredbe njegove svijem srcem i svom dušom, vršeæi rijeèi toga zavjeta napisane u toj knjizi. I sav narod prista na zavjet.
4 Mfumu inalamula wansembe wamkulu Hilikiya, ansembe othandizana naye ndi alonda a pa khomo kuti achotse mʼNyumba ya Yehova ziwiya zonse zopembedzera Baala ndi Asera ndiponso mafano a zinthu zamlengalenga. Yosiya anazitentha kunja kwa Yerusalemu, ku minda ya ku Chigwa cha Kidroni ndipo phulusa lake anapita nalo ku Beteli.
Tada zapovjedi car Helkiji poglavaru sveštenièkom i sveštenicima drugoga reda i onima koji èuvahu vrata, da iznesu iz crkve Gospodnje sve stvari koje bijahu naèinjene Valu i gaju i svoj vojsci nebeskoj; i spali ih iza Jerusalima u polju Kedronskom, i odnese pepeo od njih u Vetilj.
5 Iye anachotsa ansembe a mafano amene anayikidwa ndi mafumu a Yuda kuti azifukiza lubani ku malo opembedzera mafano a ku mizinda ya ku Yuda ndi kumalo ozungulira Yerusalemu, amene ankafukiza lubani kwa Baala, dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi zinthu zonse zamlengalenga.
I svrže sveštenike idolske koje bijahu postavili carevi Judini da kade po visinama u gradovima Judinijem i oko Jerusalima; tako i one koji kaðahu Valu, suncu i mjesecu i zvijezdama i svoj vojsci nebeskoj.
6 Anachotsa fano la Asera mʼNyumba ya Yehova napita nalo kunja kwa Yerusalemu, ku Chigwa cha Kidroni, nalitentha kumeneko. Anapera fanolo ndi kukataya phulusa lake pa manda a anthu wamba.
I iznese gaj iz doma Gospodnjega iza Jerusalima na potok Kedron, i spali ga na potoku Kedronu i satr u prah, i prosu prah na grobove sinova narodnijeh.
7 Iye anagwetsanso tinyumba ta ochita zachiwerewere, timene tinali mʼNyumba ya Yehova, kumene akazi ankalukirako mikanjo yovala popembedza Asera.
I pokvari kuæe kurvarske koje bijahu u domu Gospodnjem, u kojima žene tkahu zastiraèe za gaj.
8 Yosiya anabweretsanso ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda, nawononga malo opembedzera mafano, kuyambira ku Geba mpaka ku Beeriseba, kumene ansembe ankafukizako lubani. Anagwetsa nyumba za milungu zimene zinali pa chipata cha Yoswa, bwanamkubwa wa mzindawo, kumanzere kwa chipata cha mzinda.
I dovedavši sve sveštenike iz gradova Judinijeh oskvrni visine gdje kaðahu sveštenici od Geve do Virsaveje, i pokvari visine na vratima, i koja bijaše na ulasku na vratima Isusa zapovjednika gradskoga nalijevo od vrata gradskih.
9 Ngakhale kuti ansembe a ku malo opembedzera mafanowo sanawalole kuti atumikire pa guwa lansembe la Yehova mu Yerusalemu, koma ankadya buledi wopanda yisiti pamodzi ndi ansembe anzawo.
Ali sveštenici onijeh visina ne pristupahu k oltaru Gospodnjemu u Jerusalimu, nego jeðahu prijesne hljebove meðu braæom svojom.
10 Mfumu Yosiya anawononganso Tofeti, amene anali ku Chigwa cha Hinomu, kuti wina aliyense asagwiritse ntchito malowo popereka mwana wake wamwamuna kapena wamkazi pa moto kwa Moleki.
Oskvrni i Tofet, koji bijaše u dolini sinova Enomovijeh, da ne bi niko više vodio sina svojega ni kæeri svoje kroz oganj Molohu.
11 Anachotsa pa chipata cholowera ku Nyumba ya Yehova akavalo amene mafumu a Yuda anawapereka ngati nsembe kwa dzuwa. Akavalo anali pafupi ndi bwalo la chipinda cha mkulu wina wotchedwa Natani-Meleki. Ndipo Yosiya anatentha magaleta opembedzera dzuwa.
I ukloni konje koje bijahu postavili carevi Judini suncu od ulaska u dom Gospodnji do kuæe Natan-Meleha dvoranina, koja bijaše u Farurimu; a kola sunèana sažeže ognjem.
12 Anagwetsa maguwa amene mafumu a Yuda anawamanga pa denga pafupi ndi chipinda chapamwamba cha Ahazi, ndiponso maguwa amene Manase anamanga mʼmabwalo awiri a Nyumba ya Yehova. Yosiya anawachotsa kumeneko nawaphwanya ndi kutaya zidutswa zake mʼChigwa cha Kidroni.
I oltare na krovu sobe Ahazove, koje bijahu naèinili carevi Judini, i oltare koje bijaše naèinio Manasija u oba trijema doma Gospodnjega, pokvari car, i uzevši ih odande baci prah od njih u potok Kedron.
13 Mfumuyo inawononga malo opembedzera mafano amene ali kummawa kwa Yerusalemu cha kumpoto kwa Phiri la Chiwonongeko. Maguwawa Solomoni mfumu ya Israeli inamangira Asitoreti, fano lalikazi lonyansa la Asidoni, Kemosi, fano lonyansa la Amowabu, ndi Moleki, fano lonyansa la anthu a ku Amoni.
I visine prema Jerusalimu s desne strane na gori Maslinskoj, koje bijaše naèinio Solomun car Izrailjev Astaroti gadu Sidonskom i Hemosu gadu Moavskom i Melhomu gadu sinova Amonovijeh, oskvrni car.
14 Yosiya anaphwanya miyala ya chipembedzo ndiponso anadula mitengo ya fano la Asera ndipo anakwirira malowo ndi mafupa a anthu.
I izlomi likove i isijeèe gajeve, i mjesta njihova napuni kostiju ljudskih.
15 Ngakhalenso guwa lansembe la ku Beteli, malo opembedzera mafano amene anapanga Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli, Yosiya anawononga guwalo ndi malo opembedzera mafanowo. Iye anatentha malo opembedzera mafanowo ndi kuwapera ndipo anatenthanso fano la Asera.
I oltar, koji bješe u Vetilju, visinu, koju bješe naèinio Jerovoam sin Navatov, koji navede na grijeh Izrailja, i oltar i visinu pokvari, i spalivši visinu satr je u prah, i spali gaj.
16 Kenaka Yosiya anayangʼanayangʼana ndipo ataona manda amene anali pomwepo, mʼmbali mwa phiri, analamula kuti afukule mandawo ndi kutulutsa mafupa kuti awatenthe paguwapo kuti alidetse, potsatira mawu a Yehova amene munthu wa Mulungu analoseratu za zimenezi.
I obazrevši se Josija vidje grobove koji bijahu ondje na gori, i posla te izvadiše kosti iz grobova, i sažeže ih na oltaru i oskvrni ga, po rijeèi Gospodnjoj, koju reèe èovjek Božji, koji naprijed kaza te stvari.
17 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi chizindikiro cha manda chimene ndikuwaonawo ndi chayani?” Anthu a mu mzindamo anayankha kuti, “Ndi chizindikiro cha manda a munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda amene ananeneratu zimene inu mwalichita guwa lansembe la Beteli.”
I reèe: kakav je ono spomenik što vidim? Rekoše mu graðani: ono je grob èovjeka Božijega koji doðe iz Jude i naprijed kaza to što si uèinio na oltaru u Vetilju.
18 Mfumuyo inati, “Alekeni manda amenewo, munthu asachotse mafupa ake.” Choncho anawasiya mafupa akewo pamodzi ndi mafupa a mneneri wa ku Samariya uja.
A on reèe: ostavite ga, niko da mu ne kreæe kosti. Tako se saèuvaše kosti njegove s kostima onoga proroka koji doðe iz Samarije.
19 Monga momwe Yosiya anachitira ku Beteli, anachotsa ndi kuwononga nyumba za milungu zonse ndi malo opembedzera mafano amene mafumu anamanga mʼmizinda ya ku Samariya omwe anakwiyitsa Yehova.
I sve domove visina po gradovima Samarijskim koje naèiniše carevi Izrailjevi gnjeveæi Gospoda, pokvari Josija; i uèini s njima sve onako kako uèini u Vetilju.
20 Yosiya anapha ansembe onse amene ankatumikira ku malo opembedzera mafano, anawaphera pa maguwa awo ndi kutentha mafupa awo. Kenaka iye anapita ku Yerusalemu.
I pokla sve sveštenike visina, koji bijahu onuda, na oltarima, i sažeže kosti ljudske na njima; potom se vrati u Jerusalim.
21 Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”
Tada zapovjedi car svemu narodu govoreæi: praznujte pashu Gospodu Bogu svojemu, kao što piše u knjizi zavjetnoj.
22 Paska yotere inali isanachitikepo kuyambira nthawi ya oweruza amene anatsogolera Israeli, kapenanso nthawi yonse ya mafumu a Yuda sipanachitikenso Paska ngati imeneyo.
Jer ne bi praznovana ovako pasha od vremena sudija koje sudiše Izrailju i za sve vrijeme careva Izrailjevijeh i careva Judinijeh.
23 Koma mʼchaka cha 18 cha Mfumu Yosiya, Paska imeneyi anachitira Yehova mu Yerusalemu.
Kao što bi osamnaeste godine cara Josije praznovana pasha Gospodu u Jerusalimu.
24 Kuwonjezera apa, Yosiya anachotsa anthu a mawula, woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, milungu ya mʼnyumba, mafano ndiponso zinthu zonse zonyansa zopezeka mu Yuda ndi Yerusalemu. Iye anachita izi pokwaniritsa lamulo lolembedwa mʼbuku limene Hilikiya analipeza mʼNyumba ya Yehova.
I one što se dogovaraju s duhovima i vraèare, i likove i gadne bogove i sve gadove koji se viðahu u zemlji Judinoj i u Jerusalimu istrijebi Josija da izvrši rijeèi zakona napisane u knjizi koju naðe Helkija sveštenik u domu Gospodnjem.
25 Yosiyayo asanalowe ufumu, ngakhale atamwalira, panalibenso mfumu ina yofanana naye imene inatembenukira kwa Yehova monga anachitira, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, ndi mphamvu zake zonse, motsatira Malamulo onse a Mose.
Ni prije njega ne bješe takvoga cara, koji bi se obratio ka Gospodu svijem srcem svojim i svom dušom svojom i svom snagom svojom, sasvijem po zakonu Mojsijevu, niti poslije njega nasta taki kao on.
26 Komabe Yehova sanachotse mkwiyo wake woopsa, umene anali nawo pa Yuda chifukwa cha zonse zimene anachita Manase poputa mkwiyo wa Mulungu.
Ali se Gospod ne povrati od žestine velikoga gnjeva svojega, kojom se bješe raspalio gnjev njegov na Judu za sve draženje kojim ga bješe dražio Manasija.
27 Choncho Yehova anati, “Ndidzawachotsanso anthu a ku Yuda pamaso panga monga ndinachotsera anthu a ku Israeli ndipo ndidzawukana mzinda wa Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha, pamodzi ndi Nyumba ino imene ndinati, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo.’”
I reèe Gospod: i Judu æu odbaciti od sebe kao što sam odbacio Izrailja, i grad æu ovaj odbaciti, koji sam izabrao, Jerusalim, i dom, za koji rekoh: tu æe biti ime moje.
28 Ntchito zina za Yosiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A ostala djela Josijina i sve što je èinio, nije li zapisano u dnevniku careva Judinijeh?
29 Yosiya akanali mfumu, Farao wotchedwa Neko, mfumu ya Igupto, anapita ku Mtsinje wa Yufurate kukathandiza mfumu ya ku Asiriya. Mfumu Yosiya anapita kukachita naye nkhondo, koma Neko anakumana naye ndi kumupha ku Megido.
U njegovo vrijeme izide Faraon Nehaon car Misirski na cara Asirskoga k rijeci Efratu, i car Josija izide preda nj, a on kako ga vidje ubi ga u Megidonu.
30 Atumiki a Yosiyayo ananyamula mtembo wake mu galeta kuchokera ku Megido mpaka ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda akeake. Ndipo anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namudzoza, ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
I mrtva metnuše ga sluge njegove na kola, i odvezoše ga iz Megidona u Jerusalim, i pogreboše ga u grobu njegovu; i narod zemaljski uze Joahaza sina Josijina, i pomazaše ga i zacariše ga na mjesto oca njegova.
31 Yehowahazi anakhala mfumu ali ndi 23 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Hamutali, mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Dvadeset i tri godine bješe Joahazu kad poèe carovati, i carova tri mjeseca u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Amutala, kæi Jeremijina, iz Livne.
32 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
On èinjaše što je zlo pred Gospodom sasvijem kako su èinili oci njegovi.
33 Farao Neko anamuyika mʼndende ku Ribula mʼdziko la Hamati kuti asalamulirenso mu Yerusalemu. Farao analamula Yuda kuti azikhoma msonkho wa siliva wolemera makilogalamu 3,400, ndiponso golide wolemera makilogalamu 34.
I sveza ga Faraon Nehaon u Rivli u zemlji Ematskoj da više ne caruje u Jerusalimu, i oglobi zemlju sto talanata srebra i talanat zlata.
34 Farao Neko anayika Eliyakimu mwana wa Yosiya kuti akhale mfumu mʼmalo mwa abambo ake Yosiya, ndipo anasintha dzina lake kukhala Yehoyakimu. Koma iye anatenga Yehowahazi kupita naye ku Igupto ndipo anakafera kumeneko.
A carem postavi Faraon Nehaon Elijakima sina Josijina na mjesto Josije oca njegova, i predje mu ime Joakim; a Joahaza uze i otide u Misir, a on umrije ondje.
35 Yehoyakimu anapereka kwa Farao Neko siliva ndi golide amene anamufuna uja. Koma kuti iye apereke zimenezi, amankhometsa msonkho mʼdziko mwakemo ndipo amalandira siliva ndi golide kuchokera kwa anthu a mʼdzikomo molingana ndi chuma cha munthu aliyense.
A ono srebro i zlato dade Joakim Faraonu razrezavši na zemlju da bi dao novce po zapovijesti Faraonovoj, od svakoga uzimajuæi kako bješe cijenjen, srebro i zlato po narodu u zemlji, da da Faraonu Nehaonu.
36 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Zebuda, mwana wa Pedaya wa ku Ruma.
Dvadeset i pet godina bijaše Joakimu kad poèe carovati, i carova jedanaest godina u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Zevuda, kæi Fedajeva, iz Rume.
37 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
A on èinjaše što je zlo pred Gospodom sasvijem kako su èinili oci njegovi.

< 2 Mafumu 23 >