< 1 Mafumu 1 >

1 Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
A car David ostarje i bi vremenit, i koliko ga pokrivahu haljinama ne mogaše se zagrijati.
2 Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
Tada mu rekoše sluge njegove: neka potraže caru gospodaru našemu mladu djevojku, pa ona neka stoji pred carem i dvori ga, i na krilu neka mu spava, da se zagrijeva car gospodar naš.
3 Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
I potražiše lijepu djevojku po svijem krajevima Izrailjskim, i naðoše Avisagu Sunamku, te je dovedoše caru.
4 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
A ta djevojka bijaše vrlo lijepa, i dvoraše cara i služaše mu: ali je car ne pozna.
5 Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
A Adonija sin Agitin podiže se govoreæi: ja æu biti car. I nabavi sebi kola i konjika, i pedeset ljudi koji trèahu pred njim.
6 (Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
I otac ga nigda ne nakara, niti mu reèe: zašto radiš tako? A on bješe vrlo lijep, i mati ga rodi iza Avesaloma.
7 Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
I dogovaraše se s Joavom sinom Serujinim i s Avijatarom sveštenikom, koji pomagahu Adoniji.
8 Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
Ali Sadok sveštenik i Venaja sin Jodajev i Natan prorok i Semej i Rej i junaci Davidovi ne pristaše za Adonijom.
9 Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
Tada nakla Adonija ovaca i volova i ugojene stoke kod kamena Zoeleta, koji je kod izvora Rogila, i pozva svu braæu svoju, sinove careve, i sve ljude od Jude, sluge careve;
10 koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
Ali ne pozva Natana proroka, ni Venaje, ni ostalijeh junaka, ni Solomuna brata svojega.
11 Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
Tada reèe Natan Vitsaveji materi Solomunovoj govoreæi: jesi li èula da se zacario Adonija sin Agitin? a gospodar naš David ne zna.
12 Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
Nego sada hajde, ja æu te svjetovati kako æeš izbaviti dušu svoju i dušu sina svojega Solomuna.
13 Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
Hajde, otidi k caru Davidu i reci mu: nijesi li se ti, gospodaru moj care, zakleo sluškinji svojoj govoreæi: Solomun sin tvoj biæe car poslije mene, i on æe sjedjeti na prijestolu mojem? Zašto se dakle zacari Adonija?
14 Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
I gle, dok ti još budeš ondje govoreæi s carem, ja æu doæi za tobom, i dopuniæu tvoje rijeèi.
15 Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
I tako uðe Vitsaveja k caru u klijet. A car bijaše vrlo star; i Avisaga Sunamka dvoraše ga.
16 Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
I savivši se Vitsaveja pokloni se caru; a car joj reèe: šta æeš?
17 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
A ona mu reèe: gospodaru moj, ti si se zakleo Gospodom Bogom svojim sluškinji svojoj: Solomun sin tvoj biæe car poslije mene, i on æe sjedjeti na prijestolu mojem.
18 Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
A sada evo Adonija se zacari, a ti, gospodaru moj care, i ne znaš.
19 Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
Naklao je volova i ugojene stoke i ovaca mnogo, i pozvao sve sinove careve, i Avijatara sveštenika i Joava vojvodu; a Solomuna sluge tvojega nije pozvao.
20 Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
Sada, care gospodaru moj, oèi su svega Izrailja uprte u tebe, da im kažeš ko æe sjesti na prijesto tvoj, gospodaru moj care, poslije tebe.
21 Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
Inaèe kad gospodar moj car poèine kod otaca svojih, biæemo ja i sin moj Solomun krivi.
22 Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
I gle, dok ona još govoraše caru, doðe prorok Natan.
23 Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
I javiše caru govoreæi: evo Natana proroka. I on stupivši pred cara pokloni se caru licem do zemlje.
24 Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
I reèe Natan: care, gospodaru moj, jesi li ti kazao: Adonija æe biti car poslije mene, i on æe sjedjeti na prijestolu mojem?
25 Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
Jer otide danas i nakla volova i ugojene stoke i ovaca mnogo, i pozva sve sinove careve i vojvode i Avijatara sveštenika; i eno jedu i piju s njim i govore: da živi car Adonija.
26 Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
Mene pak, sluge tvojega, ne pozva, ni Sadoka sveštenika, ni Venaje sina Jodajeva, ni Solomuna sluge tvojega.
27 Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
Je li to car gospodar moj naredio? ne kazav sluzi svojemu ko æe sjesti na prijesto gospodara mojega cara poslije njega.
28 Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
A car David odgovori i reèe: zovite mi Vitsaveju. I ona doðe pred cara, i stade pred carem.
29 Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
Tada se zakle car govoreæi: tako da je živ Gospod, koji je izbavio dušu moju od svake nevolje,
30 ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
Kako sam ti se zakleo Gospodom Bogom Izrailjevim rekavši: Solomun sin tvoj biæe car poslije mene, i on æe sjedjeti na prijestolu mojem mjesto mene, tako æu uèiniti danas.
31 Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
Tada Vitsaveja savi se licem do zemlje i pokloni se caru, pa reèe: da živi gospodar moj car David dovijeka!
32 Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
Potom reèe car David: zovite mi Sadoka sveštenika i Natana proroka i Venaju sina Jodajeva. I oni doðoše pred cara.
33 mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
A car im reèe: uzmite sa sobom sluge gospodara svojega, i posadite Solomuna sina mojega na moju mazgu i odvedite ga do Giona;
34 Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
I neka ga ondje Sadok sveštenik i Natan prorok pomažu za cara nad Izrailjem, i zatrubite u trubu i recite: da živi car Solomun!
35 Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
Potom se vratite za njim, i on neka doðe i sjede na prijesto moj i caruje mjesto mene; jer sam njega odredio da bude voð Izrailju i Judi.
36 Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
A Venaja sin Jodajev odgovori caru i reèe: amin! neka tako reèe Gospod Bog gospodara mojega cara.
37 Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
Kako je Gospod bio s gospodarem mojim carem tako neka bude i sa Solomunom, i neka podigne prijesto njegov još više nego prijesto gospodara mojega cara Davida.
38 Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
I tako otide Sadok sveštenik i Natan prorok i Venaja sin Jodajev i Hereteji i Feleteji, i posadiše Solomuna na mazgu cara Davida i odvedoše ga do Giona.
39 Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
I Sadok sveštenik uze rog s uljem iz šatora, i pomaza Solomuna. Potom zatrubiše u trubu i sav narod reèe: da živi car Solomun!
40 Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
I sav narod poðe za njim, i narod sviraše u svirale i veseljaše se veoma da se zemlja razlijegaše od vike njihove.
41 Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
I zaèu Adonija i sve zvanice koje bijahu s njim, pošto jedoše; zaèu i Joav glas trubni, pa reèe: kaka je to vika i vreva u gradu?
42 Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
I dokle on još govoraše, gle, doðe Jonatan sin Avijatara sveštenika; i Adonija mu reèe: hodi, jer si junak i nosiš dobre glase.
43 Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
A Jonatan odgovori i reèe Adoniji: ta, gospodar naš car David postavi Solomuna carem.
44 Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
Jer car posla s njim Sadoka sveštenika i Natana proroka i Venaju sina Jodajeva, i Hereteje i Feleteje, i posadiše ga na carevu mazgu.
45 ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
I pomazaše ga Sadok sveštenik i Natan prorok kod Giona za cara, i otidoše odande veseleæi se tako da je grad uzavreo; to je vika koju èuste.
46 Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
I Solomun je veæ sjeo na carski prijesto.
47 Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
I došle su sluge careve, i blagosloviše gospodara našega cara Davida govoreæi: da Bog proslavi ime Solomunovo još veæma nego tvoje, i prijesto njegov da podigne još više nego tvoj. I pokloni se car na postelji svojoj.
48 inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
Još ovako reèe car: da je blagosloven Gospod Bog Izrailjev, koji dade danas ko æe sjedjeti na prijestolu mojemu, da vide moje oèi.
49 Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
Tada se prepadoše, i ustaše sve zvanice Adonijine, i otidoše svak svojim putem.
50 Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
A Adonija bojeæi se Solomuna usta i otide, i uhvati se za rogove oltaru.
51 Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
I javiše Solomunu govoreæi: eno, Adonija se uplašio od cara Solomuna, i eno ga, uhvatio se za rogove oltaru, i veli: neka mi se zakune car Solomun da neæe ubiti sluge svojega maèem.
52 Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
A Solomun reèe: ako bude pošten èovjek, ni dlaka s glave njegove neæe pasti na zemlju; ali ako se naðe zlo na njemu, poginuæe.
53 Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”
I tako posla car Solomun, te ga dovedoše od oltara; i kad doðe, pokloni se caru Solomunu; a Solomun mu reèe: idi kuæi svojoj.

< 1 Mafumu 1 >