< 2 Mafumu 25 >

1 Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
I tako devete godine njegova carovanja, desetoga mjeseca desetoga dana doðe Navuhodonosor car Vavilonski sa svom vojskom svojom na Jerusalim, i stadoše u oko pod njim, i naèiniše opkope oko njega.
2 Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
I grad bi opkoljen do jedanaeste godine carovanja Sedekijina.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
I devetoga dana mjeseca èetvrtoga posta velika glad u gradu, te narod zemaljski nemaše hljeba.
4 Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
Tada grad bi provaljen, a vojnici svi pobjegoše noæu na vrata izmeðu dva zida uz vrt carev; a Haldeji bijahu svuda oko grada; i car otide putem k pustinji.
5 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
Ali vojska Haldejska potjera cara, i stigoše ga u polju Jerihonskom, a sva vojska što bijaše s njim razbježe se od njega.
6 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
I uhvatiše cara, i odvedoše ga k caru Vavilonskom u Rivlu, i ondje mu sudiše.
7 Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
I sinove Sedekijine poklaše na njegove oèi, pa onda Sedekiji iskopaše oèi, i svezaše ga u dva lanca mjedena, i odvedoše ga u Vavilon.
8 Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
A sedmoga dana petoga mjeseca godine devetnaeste carovanja Navuhodonosora cara Vavilonskoga doðe u Jerusalim Nevuzardan zapovjednik stražarski, sluga cara Vavilonskoga.
9 Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
I popali dom Gospodnji i dom carski i sve domove u Jerusalimu; sve velike kuæe popali ognjem.
10 Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
I zidove Jerusalimske unaokolo razvali sva vojska Haldejska, koja bijaše sa zapovjednikom stražarskim.
11 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
A ostatak naroda što osta u gradu, i prebjege što prebjegoše k caru Vavilonskom, i ostali prosti narod odvede Nevuzardan zapovjednik stražarski.
12 Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
Samo od siromaha u zemlji ostavi zapovjednik stražarski koji æe biti vinogradari i ratari.
13 Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
I stupove mjedene što bijahu u domu Gospodnjem, i podnožja, i more mjedeno koje bijaše u domu Gospodnjem, izlomiše Haldejci, i mjed od njih odnesoše u Vavilon.
14 Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
I lonce i lopate i viljuške i kadionice i sve sudove mjedene kojima služahu, uzeše,
15 Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
I kliješta i kotliæe, što god bješe zlatno i što god bješe srebrno, uze zapovjednik stražarski,
16 Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
Dva stupa, jedno more i podnožja, što naèini Solomun za dom Gospodnji; ne bješe mjere mjedi od svijeh tijeh sudova;
17 Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
Osamnaest lakata bijaše visok jedan stup, i ozgo na njemu bijaše oglavlje mjedeno, i oglavlje bijaše visoko tri lakta, i pletenice i šipci oko oglavlja, sve od mjedi; taki bijaše i drugi stup s pletenicom.
18 Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
Uze zapovjednik stražarski i Seraju prvoga sveštenika i Sofoniju drugoga sveštenika, i tri vratara.
19 Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
A iz grada uze jednoga dvoranina, koji bijaše nad vojnicima, i pet ljudi koji stajahu pred carem, koji se naðoše u gradu, i prvoga pisara vojnièkoga, koji popisivaše narod po zemlji u vojsku, i šezdeset ljudi iz naroda zemaljskoga, koji se naðoše u gradu.
20 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
Uze ih Nevuzardan zapovjednik stražarski, i odvede k caru Vavilonskom u Rivlu.
21 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
A car ih Vavilonski pobi i pogubi u Rivli u zemlji Ematskoj. Tako bi preseljen Juda iz zemlje svoje.
22 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
A nad narodom koji osta u zemlji Judinoj, koji ostavi Navuhodonosor car Vavilonski, nad njim postavi Godoliju sina Ahikama sina Safanova.
23 Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
A kad èuše sve vojvode i ljudi njihovi da je car Vavilonski postavio Godoliju, doðoše ka Godoliji u Mispu, na ime: Ismailo sin Netanijin, i Joanan sin Karijajev, i Seraja sin Tanumetov iz Netofata, i Jazanija sin Mahatov, oni i ljudi njihovi.
24 Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
I Godolija se zakle njima i ljudima njihovijem i reèe: ne bojte se službe Haldejima; sjedite u zemlji i služite caru Vavilonskom, i biæe vam dobro.
25 Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
Ali sedmoga mjeseca doðe Ismailo sin Netanije sina Elisamova, roda carskoga, i deset ljudi s njim, i ubiše Godoliju, te pogibe; tako i Judeje i Haldeje koji bijahu s njim u Mispi.
26 Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
Tada se podiže sav narod, malo i veliko, i vojvode, te otidoše u Misir, jer se pobojaše Haldeja.
27 Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
A trideset sedme godine otkako se zarobi Joahin car Judin, dvanaestoga mjeseca, dvadeset sedmoga dana Evil-Merodah car Vavilonski iste godine zacariv se izvadi iz tamnice Joahina cara Judina.
28 Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
I lijepo govori s njim, i namjesti mu prijesto više prijestola drugih careva koji bijahu kod njega u Vavilonu.
29 Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
I promijeni mu haljine tamnièke, i on jeðaše svagda s njim svega vijeka svojega.
30 Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.
I hrana mu se jednako davaše od cara svaki dan svega vijeka njegova do smrti njegove.

< 2 Mafumu 25 >