< Psalms 64 >

1 For the leader. A psalm of David. Hear, O my God, the voice of my lament: guard my life from the dread of the foe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Hide me from villains who secretly plot, from the blustering throng of the workers of evil,
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 who have sharpened their tongue like a sword, and aimed bitter words like arrows,
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 which from ambush they launch at the blameless, shooting swiftly and unafraid.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 They strengthen their wicked purpose, they tell of the snares they have hidden, they say to themselves, ‘Who can see?’
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 They think out their crimes full cunningly hidden deep in their crafty hearts.
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 But God with his arrow will shoot them, swiftly shall they be smitten.
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 For their tongue he will bring them to ruin, all will shudder with horror at the sight of them.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 Then every person, touched to awe, as they ponder what God has wrought, will tell the tale of his deeds.
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 In the Lord shall the righteous rejoice, in him shall they take refuge; and all the true-hearted shall glory.
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!

< Psalms 64 >