< Psalms 7 >

1 A Shiggaion of David, which he sang to the Lord about Cush, the Benjamite. Lord my God, I take refuge in you. Deliver me, save me from all who pursue me;
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 or like lions they will tear me to pieces, and rend me, past hope of rescue.
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Lord, my God, if my life has been such if my hands have been stained with guilt,
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 if friends I paid back with evil, if I plundered my foes without cause,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 may the enemy chase and find me, trample my life to the ground, my honour leave in the dirt! (Selah)
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 Arise, Lord, in anger, against my foes rise in fury. Awake for my help: let justice be done.
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Gather the nations about you, and sit on your lofty throne,
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 as the Lord, the judge of the peoples. Judge me, Lord, in my innocence and according to my integrity.
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Put an end to the wrong of the wicked, protect the righteous. Searcher of hearts and minds, righteous God.
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 God is my shield: he saves the upright in heart.
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 God is a just judge, constant in righteous anger.
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 He will sharpen his sword without fail, his bow is bent and ready,
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 his deadly weapons are ready, his arrows he makes of flame.
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 The enemy who conceives evil; pregnant with mischief, giving birth to lies,
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 a pit they have made and dug; but into the hole that they made they will fall.
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 On their own heads their mischief comes back; on their own skulls their violence comes down.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 I will give thanks to the Lord for his justice, and sing to the name of the Lord Most High.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< Psalms 7 >