< Psalms 63 >

1 A psalm of David, when he was in the wilderness of Judah. O God, my God, you, you do I seek: my heart thirsts for you, my body faints for you in a parched and waterless land.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 As I in the temple have seen you, beholding your power and your glory,
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 for better than life is your kindness: my lips shall utter your praise.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 So, while I live, I will bless you, and lift up my hands in your name.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 As with marrow and fat am I feasted; with joyful lips I will praise you.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 I call you to mind on my bed, and muse on you in the night watches;
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 for you have been my help, I joyfully sing in the shadow of your wings.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 I cling close after you, your right hand holds me up.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 But those who seek after my life shall go down to the depths of the earth,
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 given o’er to the power of the sword, or as prey for jackals to devour.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 But the king shall rejoice in God: all who own his allegiance will glory. For the mouth of the false shall be stopped.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Psalms 63 >