< Psalms 65 >

1 For the leader. A psalm of David. A song. It is seemly to praise you, O God, in Zion, and to you shall the vow be performed in Jerusalem.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 O you who hear prayer, unto you shall all flesh come.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 Our sins are too mighty for us, our transgressions you only can cover them.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Happy the person who you choose to live beside you in your courts. O may we be filled with the joys of your house, of your holy temple.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 In dread deeds you loyally answer us, O God of our salvation, whom all ends of the earth put their trust in, and islands far away.
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 By your strength you establish the hills, you are armed with might;
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 you still the roaring of seas, and the turmoil of nations,
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 so that those who live at earth’s bounds are awed at your signs: the lands of the sunrise and sunset you make to ring with joy.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 You visit and water the earth; you greatly enrich her with the river of God, which is full of water. You prepare the corn thereof,
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 watering her furrows, settling her ridges; you make her soft with showers, and bless what grows thereon.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 You crown the year with your goodness, your chariot tracks drip with fatness.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 The desert pastures are lush, the hills greened with joy.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 The meadows are clothed with flocks, the valleys are covered with corn; they shout to each other and sing.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Psalms 65 >