< Masalimo 79 >

1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
O God, the nations have come into thine inheritance. They have defiled thy holy temple. They have laid Jerusalem in heaps.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
They have given the dead bodies of thy servants to be food to the birds of the heavens, the flesh of thy sanctified to the beasts of the earth.
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
They have shed their blood like water round about Jerusalem, and there was none to bury them.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
We have become a reproach to our neighbors, a scoffing and derision to those who are round about us.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
How long, O Jehovah? Will thou be angry forever? Shall thy jealousy burn like fire?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Pour out thy wrath upon the nations that do not know thee, and upon the kingdoms that do not call upon thy name.
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
For they have devoured Jacob, and laid waste his habitation.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Do not remember against us the iniquities of our forefathers. Let thy tender mercies speedily meet us, for we are brought very low.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Help us, O God of our salvation, for the glory of thy name. And deliver us, and forgive our sins, for thy name's sake.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Why should the nations say, Where is their God? Let the avenging of the blood of thy servants which is shed be known among the nations in our sight.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
Let the sighing of the prisoner come before thee. According to the greatness of thy power preserve thou those who are appointed to death,
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
and render to our neighbors sevenfold into their bosom their reproach with which they have reproached thee, O Lord,
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
so we thy people and sheep of thy pasture will give thee thanks forever. We will show forth thy praise to all generations.

< Masalimo 79 >