< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Give ear, O my people, to my law. Incline your ears to the words of my mouth.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
I will open my mouth in parables. I will utter dark sayings of old,
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
which we have heard and known, and our fathers have told us.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
We will not hide them from their sons, telling to the generation to come the praises of Jehovah, and his strength, and his wondrous works that he has done.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
For he established a testimony in Jacob, and appointed a law in Israel, which he commanded our fathers, that they should make them known to their sons,
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
that the generation to come might know, even the sons who should be born, who should arise and tell to their sons,
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
that they might set their hope in God, and not forget the works of God, but keep his commandments,
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
and might not be as their fathers: a stubborn and rebellious generation, a generation that set not their heart aright, and whose spirit was not steadfast with God.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
The sons of Ephraim, being armed and carrying bows, turned back in the day of battle.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
They kept not the covenant of God, and refused to walk in his law.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
And they forgot his doings, and his wondrous works that he had shown them.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
He did marvelous things in the sight of their fathers, in the land of Egypt, in the field of Zoan.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
He divided the sea, and caused them to pass through. And he made the waters to stand as a heap.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
In the daytime also he led them with a cloud, and all the night with a light of fire.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
He split rocks in the wilderness, and gave them drink abundantly as out of the depths.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
He brought streams also out of the rock, and caused waters to run down like rivers.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Yet they went on to still sin against him, to rebel against the Most High in the desert.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
And they challenged God in their heart by asking food according to their desire.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
Yea, they spoke against God. They said, Can God prepare a table in the wilderness?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Behold, he smote the rock, so that waters gushed out, and streams overflowed. Can he give bread also? Will he provide flesh for his people?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Therefore Jehovah heard, and was angry. And a fire was kindled against Jacob, and anger also went up against Israel,
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
because they did not believe in God, and did not trust in his salvation.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Yet he commanded the skies above, and opened the doors of heaven,
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
and he rained down manna upon them to eat, and gave them food from heaven.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Man ate the bread of the mighty. He sent them food to the full.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
He caused the east wind to blow in the heavens, and by his power he guided the south wind.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
He also rained flesh upon them as the dust, and winged birds as the sand of the seas.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
And he let it fall in the midst of their camp round about their habitations.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
So they ate, and were well filled, and he gave them their own desire.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
They were not estranged from that which they desired. Their food was yet in their mouths
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
when the anger of God went up against them, and killed of the fattest of them, and smote down the young men of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
For all this they still sinned, and did not believe in his wondrous works.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Therefore he consumed their days in vanity, and their years in terror.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
When he killed them, then they inquired after him, and they returned and sought God earnestly.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
And they remembered that God was their rock, and the Most High God their redeemer.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
But they flattered him with their mouth, and lied to him with their tongue.
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
For their heart was not right with him, nor were they faithful in his covenant.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
But he, being merciful, forgave iniquity, and destroyed not. Yea, many a time he turned his anger away, and did not stir up all his wrath.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
And he remembered that they were but flesh, a wind that passes away, and comes not again.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
How often they rebelled against him in the wilderness, and grieved him in the desert!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
And they turned again and challenged God, and provoked the Holy One of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
They did not remember his hand, nor the day when he redeemed them from the adversary,
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
how he set his signs in Egypt, and his wonders in the field of Zoan,
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
and turned their rivers into blood, and their streams, so that they could not drink.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sent among them swarms of flies, which devoured them, and frogs, which destroyed them.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
He also gave their increase to the caterpillar, and their labor to the locust.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
He destroyed their vines with hail, and their sycamore trees with frost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
He also gave over their cattle to the hail, and their flocks to hot thunderbolts.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
He cast upon them the fierceness of his anger, wrath, and indignation, and trouble, a band of agents of evil.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He made a path for his anger. He spared not their soul from death, but gave their life over to the pestilence,
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
and smote all the firstborn in Egypt, the chief of their strength in the tents of Ham.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
But he led forth his own people like sheep, and guided them in the wilderness like a flock.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
And he led them safely, so that they feared not, but the sea overwhelmed their enemies.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
And he brought them to the border of his sanctuary, to this mountain, which his right hand had gotten.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
He also drove out the nations before them, and allotted them for an inheritance by line, and made the tribes of Israel to dwell in their tents.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Yet they challenged and rebelled against the Most High God, and kept not his testimonies,
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
but turned back, and dealt treacherously like their fathers. They were turned aside like a deceitful bow.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
For they provoked him to anger with their high places, and moved him to jealousy with their graven images.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
When God heard, he was angry, and greatly abhorred Israel,
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
so that he forsook the tabernacle of Shiloh, the tent which he placed among men,
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
and delivered their strength into captivity, and their glory into the adversary's hand.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
He also gave his people over to the sword, and was angry with his inheritance.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Fire devoured their young men, and their virgins had no marriage-song.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Their priests fell by the sword, and their widows made no lamentation.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Then the Lord awoke as out of sleep, like a mighty man who shouts because of wine.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
And he smote his adversaries backward. He put them to a perpetual reproach.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Moreover he refused the tent of Joseph, and chose not the tribe of Ephraim,
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
but chose the tribe of Judah, the mount Zion which he loved.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
And he built his sanctuary like the heights, like the earth which he has established forever.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
He also chose David his servant, and took him from the sheepfolds.
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
He brought him from following the ewes that have their young, to be the shepherd of Jacob his people, and Israel his inheritance.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
So he was their shepherd according to the integrity of his heart, and guided them by the skillfulness of his hands.

< Masalimo 78 >