< Masalimo 74 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
O God, why have thou cast off forever? Why does thine anger smoke against the sheep of thy pasture?
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Remember thy congregation, which thou have gotten of old, which thou have redeemed to be the tribe of thine inheritance, and mount Zion, at which thou have dwelt.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
Lift up thy feet to the perpetual ruins, all the evil that the enemy has done in the sanctuary.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Thine adversaries have roared in the midst of thine assembly. They have set up their ensigns for signs.
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
They seemed as men who lifted up axes upon a thicket of trees.
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
And now they break down all the carved work of it with hatchet and hammers.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
They have set thy sanctuary on fire. They have profaned the dwelling-place of thy name to the ground.
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
They said in their heart, Let us make havoc of them altogether. They have burned up all the meeting-places of God in the land.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
We do not see our signs. There is no more any prophet, nor is there among us he who knows how long.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
How long, O God, shall the adversary reproach? Shall the enemy blaspheme thy name forever?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Why do thou draw back thy hand, even thy right hand? Remove it from the midst of thy bosom.
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
Yet God is my King of old, working salvation in the midst of the earth.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
Thou divided the sea by thy strength. Thou break the heads of the sea-monsters in the waters.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
Thou break the heads of leviathan in pieces. Thou gave him to be food to the people inhabiting the wilderness.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
Thou split fountain and flood. Thou dried up mighty rivers.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
The day is thine; the night is also thine. Thou have prepared the light and the sun.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
Thou have set all the borders of the earth. Thou have made summer and winter.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Remember this, that the enemy has reproached, O Jehovah, and that a foolish people has blasphemed thy name.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
O deliver not the soul of thy turtle-dove to the wild beast. Forget not the life of thy poor forever.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Have respect to the covenant, for the dark places of the earth are full of the habitations of violence.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
O let not he who is oppressed return ashamed. Let a poor and needy man praise thy name.
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Arise, O God, plead thine own cause. Remember how the foolish man reproaches thee all the day.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
Forget not the voice of thine adversaries. The tumult of those who rise up against thee ascends continually.

< Masalimo 74 >