< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
Surely God is good to Israel, to such as are pure in heart.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
But as for me, my feet were almost gone. My steps had well nigh slipped.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
For I was envious of the arrogant when I saw the prosperity of the wicked.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
For there are no pangs in their death, but their strength is firm.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
They are not in trouble as other men, nor are they plagued like other men.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Therefore pride is as a chain around their neck. Violence covers them as a garment.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Their eyes stand out with fatness. They have more than heart could wish.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
They scoff, and in wickedness utter oppression. They speak loftily.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
They have set their mouth in the heavens, and their tongue walks through the earth.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Therefore his people return here, and waters of a full cup are drained by them.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
And they say, How does God know? And is there knowledge in the Most High?
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Behold, these are the wicked, and those who always prosper. They have possessed wealth.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
Surely in vain I have cleansed my heart, and washed my hands in innocence,
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
for all the day long I have been plagued, and chastened every morning.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
If I had said, I will speak thus, behold, I would have dealt treacherously with the generation of thy sons.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
When I thought how I might understand this, it was too painful for me,
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
until I went into the sanctuary of God, and considered their latter end.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Surely thou set them in slippery places. Thou cast them down to destruction.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
How they have become a desolation in a moment! They are utterly consumed with terrors.
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
As a dream from awakening, O Lord, when thou waken, thou will despise their form.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
For my soul was grieved, and I was pricked in my heart.
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
So I was brutish, and ignorant. I was a beast before thee.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Nevertheless I am continually with thee. Thou have held my right hand.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Thou will guide me with thy counsel, and afterward receive me to glory.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Whom have I in heaven? And there is none upon earth that I desire besides thee.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
My flesh and my heart fails, but God is the strength of my heart and my portion forever.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
For, lo, those who are far from thee shall perish. Thou have destroyed all those who go a whoring from thee.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
But it is good for me to draw near to God. I have made the lord Jehovah my refuge, that I may tell of all thy works.

< Masalimo 73 >