< Masalimo 55 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
Give ear to my prayer, O God, and hide not thyself from my supplication.
2 mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
Attend to me, and answer me. I am restless in my complaint, and moan,
3 chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
because of the voice of the enemy, because of the oppression of the wicked. For they cast iniquity upon me, and in anger they persecute me.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
My heart is greatly pained within me, and the terrors of death have fallen upon me.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
Fearfulness and trembling have come upon me, and horror has overwhelmed me.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
And I said, O that I had wings like a dove! Then I would fly away, and be at rest.
7 Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
Lo, then I would wander far off. I would lodge in the wilderness. (Selah)
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
I would hasten myself to a shelter from the stormy wind and tempest.
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
Destroy, O Lord, divide their tongue, for I have seen violence and strife in the city.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
Day and night they go about it, upon the walls of it. Iniquity and mischief also are in the midst of it.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
Wickedness is in the midst of it. Oppression and deceit depart not from its streets.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
For it was not an enemy who reproached me. Then I could have borne it. Neither was it he who hated me that magnified himself against me. Then I would have hid myself from him.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
But it was thou, a man my equal, my companion, and my familiar friend.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
We took sweet counsel together. We walked in the house of God with the throng.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
Let death come suddenly upon them. Let them go down alive into Sheol. For wickedness is in their dwelling, in the midst of them. (Sheol h7585)
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
As for me, I will call upon God, and Jehovah will save me.
17 Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
Evening, and morning, and at noonday, I will complain and moan. And he will hear my voice.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
He has redeemed my soul in peace from the battle that was against me, for there were many by me.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
God will hear, and respond to them, (even he who abides of old), (Selah) men who have no changes, and who fear not God.
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
He has put forth his hands against such as were at peace with him. He has profaned his covenant.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
His mouth was smooth as butter, but his heart was war. His words were softer than oil, yet they were drawn swords.
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
(Cast thy burden upon Jehovah, and he will sustain thee. He will never allow the righteous man to be moved.)
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.
But thou, O God, will bring them down into the pit of destruction. Bloodthirsty and deceitful men shall not live out half their days, but I will trust in thee.

< Masalimo 55 >