< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
The heavens declare the glory of God, and the firmament shows his handiwork.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Day to day utters speech, and night to night shows knowledge.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
There is no speech nor language in which their voice is not heard.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Their line has gone out through all the earth, and their words to the end of the world. In them he has set a tabernacle for the sun,
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
which is as a bridegroom coming out of his chamber, and rejoices as a strong man to run his course.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
His going forth is from the end of the heavens, and his circuit to the ends of it, and there is nothing hid from the heat of it.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
The law of Jehovah is perfect, restoring the soul. The testimony of Jehovah is sure, making a simple man wise.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
The precepts of Jehovah are right, rejoicing the heart. The commandment of Jehovah is pure, enlightening the eyes.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
The fear of Jehovah is clean, enduring forever. The ordinances of Jehovah are true, and righteous altogether.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
More to be desired are they than gold, yea, than much fine gold. Sweeter also than honey and the droppings of the honeycomb.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
Moreover by them thy servant is warned. In keeping them there is great reward.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Who can discern his errors? Clear thou me from hidden faults.
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
Keep back thy servant also from presumptuous sins. Let them not have dominion over me. Then I shall be upright, and I shall be clear from great transgression.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
Let the words of my mouth and the meditation of my heart be acceptable in thy sight, O Jehovah, my rock, and my redeemer.

< Masalimo 19 >