< Masalimo 16 >

1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
Preserve me, O God, for in thee do I take refuge.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Thou my soul have said to Jehovah, Thou are my Lord. I have no good beyond thee.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
As for the sanctified who are in the earth, they are the excellent in whom is all my delight.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
Their sorrows shall be multiplied who give gifts for another god. Their drink offerings of blood I will not offer, nor take their names upon my lips.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
Jehovah is the portion of my inheritance and of my cup. Thou maintain my lot.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
The lines are fallen to me in pleasant places. Yea, I have a fine heritage.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
I will bless Jehovah, who has given me counsel. Yea, my heart instructs me in the night seasons.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
I beheld Jehovah always before me. Because he is at my right hand, I shall not be moved.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
Therefore my heart is glad, and my glory rejoices. My flesh also shall dwell in hope.
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol h7585)
For thou will not leave my soul to Sheol, nor will thou allow thy holy man to see corruption. (Sheol h7585)
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Thou made known to me the path of life. Thou will fill me of joy with thy countenance.

< Masalimo 16 >