< Masalimo 146 >

1 Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Praise ye Jehovah. Praise Jehovah, O my soul.
2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
While I live I will praise Jehovah. I will sing praises to my God while I have any being.
3 Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
Put not your trust in rulers, nor in the son of man, in whom there is no help.
4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
His breath goes forth, he returns to his earth. In that very day his thoughts perish.
5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
Happy is he who has the God of Jacob for his help, whose hope is in Jehovah his God,
6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
who made heaven and earth, the sea, and all that is in them, who keeps truth forever,
7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
who executes justice for the oppressed, who gives food to the hungry. Jehovah releases the prisoners.
8 Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
Jehovah opens the eyes of the blind. Jehovah raises up those who are bowed down. Jehovah loves the righteous.
9 Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
Jehovah preserves the sojourners. He upholds the fatherless and widow. But the way of the wicked he turns upside down.
10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.
Jehovah will reign forever, thy God, O Zion, to all generations. Praise ye Jehovah.

< Masalimo 146 >