< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Praise ye Jehovah. Praise ye the name of Jehovah. Praise, O ye servants of Jehovah,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
ye who stand in the house of Jehovah, in the courts of the house of our God.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Praise ye Jehovah, for Jehovah is good. Sing praises to his name, for it is pleasant.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For Jehovah has chosen Jacob to himself, Israel for his own possession.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
For I know that Jehovah is great, and that our Lord is above all gods.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Whatever Jehovah pleased, that he has done, in heaven and in earth, in the seas and in all deeps,
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
who causes the vapors to ascend from the ends of the earth, who makes lightnings for the rain, who brings forth the wind out of his treasuries,
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
who smote the firstborn of Egypt, both of man and beast,
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
who sent signs and wonders into the midst of thee, O Egypt, upon Pharaoh, and upon all his servants,
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
who smote many nations, and killed mighty kings-
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon king of the Amorites, and Og king of Bashan, and all the kingdoms of Canaan-
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
and gave their land for a heritage, a heritage to Israel his people.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Thy name, O Jehovah, is forever, thy memorial, O Jehovah, throughout all generations.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For Jehovah will judge his people, and will relent concerning his servants.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The idols of the nations are silver and gold, the work of men's hands.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
They have mouths, but they speak not. They have eyes, but they see not.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
They have ears, but they hear not, nor is there any breath in their mouths.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Those who make them shall be like them, yea, everyone who trusts in them.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
O house of Israel, bless ye Jehovah. O house of Aaron, bless ye Jehovah.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
O house of Levi, bless ye Jehovah. Ye who fear Jehovah, bless ye Jehovah.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Blessed be Jehovah out of Zion, who dwells at Jerusalem. Praise ye Jehovah.

< Masalimo 135 >