< Masalimo 122 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
I was glad when they said to me, Let us go to the house of Jehovah.
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Our feet are standing inside thy gates, O Jerusalem.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem, that is built as a city that is compact together,
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
where the tribes go up, even the tribes of Jehovah, for an ordinance for Israel, to give thanks to the name of Jehovah.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
For there thrones are set for judgment, the thrones of the house of David.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Pray for the peace of Jerusalem. They shall prosper who love thee.
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Peace be within thy walls, and prosperity within thy palaces.
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
For my brothers and companions' sakes I will now say, Peace be within thee.
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
For the sake of the house of Jehovah our God I will seek thy good.

< Masalimo 122 >