< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
He who, being often reproved, hardens his neck shall suddenly be destroyed, and that without remedy.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
When the righteous are increased, the people rejoice, but when a wicked man bears rule, the people sigh.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
He who loves wisdom delights his father, but he who keeps company with harlots wastes his substance.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
By justice the king establishes the land, but he who exacts gifts overthrows it.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
A man who flatters his neighbor spreads a net for his steps.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
In the transgression of an evil man there is a snare, but a righteous man sings and rejoices.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
A righteous man takes knowledge of the cause of the poor. A wicked man has no such understanding to know.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Scoffers set a city in a flame, but wise men turn away wrath.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
If a wise man has a controversy with a foolish man, whether he be angry or laugh, there will be no rest.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
Bloodthirsty men hate him who is perfect, but the upright seek his soul.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
A fool utters all his anger, but a wise man keeps it back and calms it.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
If a ruler hearkens to falsehood, all his servants are wicked.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
The poor man and the oppressor meet together. Jehovah enlightens the eyes of them both.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
The king who faithfully judges the poor, his throne shall be established forever.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
The rod and reproof give wisdom, but a child left to himself causes shame to his mother.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
When the wicked are increased, transgression increases, but the righteous shall look upon their fall.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Correct thy son, and he will give thee rest, yea, he will give delight to thy soul.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Where there is no vision, the people cast off restraint, but he who keeps the law, happy is he.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
A servant will not be corrected by words, for though he understands, he will not give heed.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
See thou a man who is hasty in his words? There is more hope for a fool than for him.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
He who brings up his servant gently from childhood shall have him become a son at the last.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
An angry man stirs up strife, and a wrathful man abounds in transgression.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
A man's pride shall bring him low, but he who is of a lowly spirit shall obtain honor.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
He who is partner with a thief hates his own soul; he hears the adjuration and utters nothing.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
The fear of man brings a snare, but he who puts his trust in Jehovah shall be safe.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Many seek the ruler's favor, but a man's justice is from Jehovah.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
An unjust man is an abomination to the righteous, and he who is upright in the way is an abomination to a wicked man.

< Miyambo 29 >