< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
When thou sit to eat with a ruler, consider diligently him who is before thee,
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
and put a knife to thy throat if thou be a man given to appetite.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Be not desirous of his dainties, since they are deceitful food.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Weary not thyself to be rich. Out of thine own wisdom, cease.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Will thou set thine eyes upon that which is not? For it certainly makes itself wings, like an eagle that flies toward heaven.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Eat thou not the bread of an evil eye, nor desire thou his dainties.
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
For as he thinks within himself, so is he. Eat and drink, he says to thee, but his heart is not with thee.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
The morsel which thou have eaten thou shall vomit up, and lose thy sweet words.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Speak not in the hearing of a fool, for he will despise the wisdom of thy words.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Remove not the ancient landmark. And enter not into the fields of the fatherless,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
for their Redeemer is strong. He will plead their cause against thee.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Apply thy heart to instruction, and thine ears to the words of knowledge.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Withhold not correction from the child, for if thou beat him with the rod, he will not die.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Thou shall beat him with the rod, and shall deliver his soul from Sheol. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
My son, if thy heart be wise, my heart will be glad, even mine.
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
Yea, my heart will rejoice when thy lips speak right things.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Let not thy heart envy sinners, but be thou in the fear of Jehovah all the day long.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
For surely there is a reward, and thy hope shall not be cut off.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Hear thou, my son, and be wise, and guide thy heart in the way.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Be not among winebibbers, among gluttonous eaters of flesh.
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
For the drunkard and the glutton shall come to poverty, and drowsiness will clothe a man with rags.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Hearken to thy father who begot thee, and despise not thy mother when she is old.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Buy the truth, and do not sell it, yea, wisdom, and instruction, and understanding.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
The father of a righteous man will greatly rejoice, and he who begets a wise son will have joy of him.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Let thy father and thy mother be glad, and let her who bore thee rejoice.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
My son, give me thy heart, and let thine eyes delight in my ways.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
For a harlot is a deep ditch, and an interloping woman is a narrow pit.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Yea, she lies in wait as a robber, and increases the treacherous among men.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Who has woe? Who has sorrow? Who has contentions? Who has complaining? Who has wounds without cause? Who has redness of eyes?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Those who tarry long at the wine. Those who go to seek out mixed wine.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Look not thou upon the wine when it is red, when it sparkles in the cup, when it goes down smoothly.
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
At the end it bites like a serpent, and stings like an adder.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Thine eyes shall behold strange things, and thy heart shall utter perverse things.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Yea, thou shall be as he who lies down in the midst of the sea, or as he who lies upon the top of a mast.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
They have stricken me, thou shall say, and I was not hurt. They have beaten me, and I did not feel it. When shall I awake? I will seek it yet again.

< Miyambo 23 >