< Miyambo 30 >

1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
The words of Agur the son of Jakeh, the oracle. The man says to Ithiel, to Ithiel and Ucal:
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Surely I am more brutish than any man, and have not the understanding of a man,
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
and I have not learned wisdom, nor have I the knowledge of the Holy.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Who has ascended up into heaven, and descended? Who has gathered the wind in his fists? Who has bound the waters in his garment? Who has established all the ends of the earth? What is his name, and what is his son's name, if thou know?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Every word of God is tried. He is a shield to those who take refuge in him.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
Add thou not to his words, lest he reprove thee, and thou be found a liar.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
Two things I have asked of thee, deny me not before I die:
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Remove far from me falsehood and lies. Give me neither poverty nor riches; feed me with the food that is needful for me,
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
lest I be full, and deny thee, and say, Who is Jehovah? or lest I be poor, and steal, and use the name of my God profanely.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
Slander not a servant to his master, lest he curse thee, and thou be held guilty.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
There is a generation who curses their father, and does not bless their mother.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
There is a generation who are pure in their own eyes, and yet are not washed from their filthiness.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
There is a generation, O how lofty are their eyes, and their eyelids are lifted up.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
There is a generation whose teeth are swords, and their jaw teeth, knives, to devour the poor from off the earth, and the needy from among men.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
The leach has two daughters, crying, Give, give. There are three things that are never satisfied, yea, four that do not say, Enough:
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
Sheol, and the barren womb, the earth that is not satisfied with water, and the fire that does not say, Enough. (Sheol h7585)
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
The eye that mocks at his father, and despises to obey his mother, the ravens of the valley shall pick it out, and the young eagles shall eat it.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
There are three things which are too wonderful for me, yea, four which I know not:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
The way of an eagle in the air, the way of a serpent upon a rock, the way of a ship in the midst of the sea, and the way of a man with a maiden.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
So is the way of an adulterous woman: She eats, and wipes her mouth, and says, I have done no iniquity.
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
For three things the earth trembles, and for four, which it cannot bear:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
For a servant when he is king, and a fool when he is filled with food,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
for a hateful woman when she is married, and a handmaid that is heir to her mistress.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
There are four things which are little upon the earth, but they are exceedingly wise:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
The ants are a people not strong, yet they prepare their food in the summer,
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
the conies are but a feeble folk, yet they make their houses in the rocks,
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
the locusts have no king, yet they go forth all of them by bands,
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
the lizard takes hold with her hands, yet she is in kings' palaces.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
There are three things which are stately in their march, yea, four which are stately in going:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
The lion, which is mightiest among beasts, and turns not away from any,
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
the greyhound, also the he-goat, and the king against whom there is no rising up.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
If thou have done foolishly in lifting up thyself, or if thou have thought evil, lay thy hand upon thy mouth.
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
For the churning of milk brings forth butter, and the wringing of the nose brings forth blood, so the forcing of wrath brings forth strife.

< Miyambo 30 >