< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Be not thou envious against evil men, nor desire to be with them.
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
For their heart meditates oppression, and their lips talk of mischief.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Through wisdom a house is built, and by understanding it is established,
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
and by knowledge the chambers are filled with all precious and pleasant riches.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
A wise man is strong, yea, a man of knowledge increases might.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
For by wise guidance thou shall make thy war, and in the multitude of counselors there is safety.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Wisdom is too high for a fool. He opens not his mouth in the gate.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
He who devises to do evil, men shall call him a mischief-maker.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
The thought of folly is sin. And the scoffer is an abomination to men.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
If thou faint in the day of adversity, thy strength is small.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Deliver those who are carried away to death, and hold thou back those who are ready to be slain.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
If thou say, Behold, we did not know this, Does not he who weighs the hearts consider it? And he who keeps thy soul, does he not know it? And shall not he render to every man according to his work?
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
My son, eat thou honey, for it is good, and the droppings of the honeycomb, which are sweet to thy taste,
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
so the knowledge of wisdom is to thy soul. If thou have found it, then there shall be a reward, and thy hope shall not be cut off.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Lay not in wait, O wicked man, against the habitation of the righteous. Do not destroy his resting place.
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
For a righteous man falls seven times, and rises up again, but the wicked are overthrown by calamity.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Rejoice not when thine enemy falls, and let not thy heart be glad when he is overthrown,
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
lest Jehovah see it, and it displease him, and he turn away his wrath from him.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Fret not thyself because of evildoers, nor be thou envious at the wicked.
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
For there shall be no reward to the evil man. The lamp of the wicked shall be put out.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
My son, fear thou Jehovah and the king, and do not associate with those who are given to change.
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
For their calamity shall rise suddenly, and the destruction from them both, who knows it?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
These also are from the wise: To have respect of persons in judgment is not good.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
He who says to a wicked man, Thou are righteous, peoples shall curse him, nations shall abhor him.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
But to those who rebuke him shall be delight, and a good blessing shall come upon them.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
He who gives a right answer kisses the lips.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Prepare thy work outside, and make it ready for thee in the field, and afterwards build thy house.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Be not a witness against thy neighbor without cause, and deceive not with thy lips.
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Say not, I will do so to him as he has done to me; I will render to the man according to his work.
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
I went by the field of the sluggard, and by the vineyard of the man void of understanding.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
And, lo, it was all grown over with thorns. The face of it was covered with nettles, and the stone wall of it was broken down.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Then I beheld, and considered well. I saw, and received instruction:
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
Yet a little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to sleep,
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
so thy poverty shall come as a robber, and thy want as an armed man.

< Miyambo 24 >