< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
The king's heart is in the hand of Jehovah as streams of water. He turns it wherever he will.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Every way of a man is right in his own eyes, but Jehovah weighs the hearts.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
To do righteousness and justice is more acceptable to Jehovah than sacrifice.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
A high look, and a proud heart, even the lamp of the wicked, is sin.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
The thoughts of a diligent man lead only to abundance, but everyone who is hasty, only to want.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
The getting of treasures by a lying tongue is a vapor driven to and fro by those who seek death.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
The violence of the wicked shall sweep them away, because they refuse to do justice.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
The way of him who is laden with guilt is exceedingly crooked, but as for a pure man, his work is right.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
It is better to dwell in the corner of the housetop, than with a contentious woman in a wide house.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
The soul of a wicked man desires evil. His neighbor finds no favor in his eyes.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
When a scoffer is punished, a simple man is made wise, and when a wise man is instructed, he receives knowledge.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
A righteous man considers the house of the wicked: the wicked are overthrown to ruin.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
He who stops his ears at the cry of a poor man, he also shall cry, but shall not be heard.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
A gift in secret pacifies anger, and a present in the bosom, strong wrath.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
It is joy to the righteous to do justice, but it is a destruction to the workers of iniquity.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
The man who wanders out of the way of understanding shall rest in the assembly of the dead.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
He who loves pleasure shall be a poor man. He who loves wine and oil shall not be rich.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
A wicked man is a ransom for a righteous man, and the treacherous dealer for the upright.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
It is better to dwell in a desert land, than with a contentious and fretful woman.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
There is precious treasure and oil in the dwelling of a wise man, but a foolish man swallows it up.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
He who follows after righteousness and kindness finds life, righteousness, and honor.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
A wise man scales the city of the mighty, and brings down the strength of the confidence of it.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
He who keeps his mouth and his tongue keeps his soul from troubles.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
The proud and haughty man, scoffer is his name. He works in the arrogance of pride.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
The desire of the sluggard kills him, for his hands refuse to labor.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
There is he who covets greedily all the day long, but the righteous gives and does not withhold.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
The sacrifice of the wicked is an abomination. How much more when he brings it with a wicked mind!
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
A false witness shall perish, but the man who hears shall speak so as to endure.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
A wicked man hardens his face, but as for an upright man, he establishes his ways.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
There is no wisdom nor understanding nor counsel against Jehovah.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
The horse is prepared against the day of battle, but victory is from Jehovah.

< Miyambo 21 >