< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Wine is a mocker, strong drink a brawler, and whoever errs thereby is not wise.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
The terror of a king is as the roaring of a lion. He who provokes him to anger sins against his own life.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
It is an honor for a man to keep aloof from strife, but every fool will be quarrelling.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
The sluggard will not plow because of the winter. Therefore he shall beg in harvest, and have nothing.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Purpose in the heart of man is deep water, but a man of understanding will draw it out.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Most men will proclaim every one his own goodness, but a faithful man who can find?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
A righteous man who walks in his integrity, blessed are his sons after him.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
A king who sits on the throne of judgment scatters away all evil with his eyes.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Who can say, I have made my heart clean. I am pure from my sin?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Diverse weights, and diverse measures, both of them alike are an abomination to Jehovah.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Even a child makes himself known by his doings, whether his work be pure, and whether it be right.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
The hearing ear, and the seeing eye, Jehovah has made even both of them.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Love not sleep, lest thou come to poverty. Open thine eyes, and thou shall be satisfied with bread.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
It is bad, it is bad, says the buyer, but when he is gone his way, then he boasts.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
There is gold, and abundance of rubies, but the lips of knowledge are a precious jewel.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Take his garment who is surety for a stranger, and hold him in pledge for foreigners.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Bread of falsehood is sweet to a man, but afterwards his mouth shall be filled with gravel.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Every purpose is established by counsel, and by wise guidance make thou war.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
He who goes about as a tale-bearer reveals secrets. Therefore do not associate with him who opens wide his lips.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
He who curses his father or his mother, his lamp shall be put out in blackness of darkness.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
An inheritance gotten hastily at the beginning shall not be blessed in the end.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Say thou not, I will recompense evil. Wait for Jehovah, and he will save thee.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Diverse weights are an abomination to Jehovah, and a false balance is not good.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
A man's goings are of Jehovah, how then can man understand his way?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
It is a snare to a man to say rashly, It is holy. And to make inquiry after vows.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
A wise king winnows the wicked, and brings the wheel over them.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
The spirit of man is the lamp of Jehovah, searching all his innermost parts.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Kindness and truth preserve the king, and his throne is upheld by kindness.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
The glory of young men is their strength, and the beauty of old men is the hoary head.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Stripes that wound cleanse away evil, and strokes, the innermost parts.

< Miyambo 20 >