< Miyambo 19 >

1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Better is a poor man who walks in his integrity than he who is perverse in his lips and is a fool.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Also, that the soul be without knowledge is not good. And he who hastens with his feet sins.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
The foolishness of a man subverts his way, and his heart rages against Jehovah.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Wealth adds many friends, but a poor man is separated from his friend.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
A false witness shall not be unpunished, and he who utters lies shall not escape.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Many will entreat the favor of a generous man, and every man is a friend to him who gives gifts.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
All the brothers of a poor man regard him inferior, how much more do his friends go far from him! He pursues with words, but they are gone.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
He who gets wisdom loves his own soul. He who keeps understanding shall find good.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
A false witness shall not be unpunished, and he who utters lies shall perish.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Luxurious living is not fitting for a fool, much less for a servant to have rule over rulers.
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
The discretion of a man makes him slow to anger, and it is his glory to pass over a transgression.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
The king's wrath is as the roaring of a lion, but his favor is as dew upon the grass.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
A foolish son is the calamity of his father, and the contentions of a wife are a continual dropping.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
House and riches are an inheritance from fathers, but a prudent wife is from Jehovah.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Slothfulness casts into a deep sleep, and the idle soul shall suffer hunger.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
He who keeps the commandment keeps his soul. He who is careless of his ways shall die.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
He who has pity upon a poor man lends to Jehovah, and he will repay him his good deed.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Chasten thy son while there is hope, and let not thy soul spare for his crying.
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
A man of great wrath shall bear the penalty, for if thou deliver him, thou must do it yet again.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Hear counsel, and receive instruction, that thou may be wise in thy latter end.
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
There are many devices in a man's heart, but the counsel of Jehovah, that shall stand.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
That which makes a man to be desired is his kindness, and a poor man is better than a liar.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
The fear of Jehovah is life to a man, and he shall abide satisfied. He shall not be visited with evil.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
The sluggard buries his hand in the dish, and will not so much as bring it to his mouth again.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Smite a scoffer, and a simple man will learn prudence. And reprove him who has understanding, and he will understand knowledge.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
He who does violence to his father, and chases away his mother, is a son that causes shame and brings reproach.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
To err from the words of knowledge, cease, my son, to hear instruction.
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
A worthless witness mocks at justice, and the mouth of the wicked swallows iniquity.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Judgments are prepared for scoffers, and stripes for the back of fools.

< Miyambo 19 >