< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
He who desires to separate himself seeks excuses, and rages against all sound wisdom.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
A fool has no delight in understanding, but only that his heart may reveal itself.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
When a wicked man comes, contempt also comes, and with disgrace, reproach.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
The words of a man's mouth are deep waters. The wellspring of wisdom is a flowing brook.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
To respect the person of a wicked man is not good, nor to turn aside a righteous man in judgment.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
A fool's lips enter into contention, and his mouth calls for stripes.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
A fool's mouth is his destruction, and his lips are the snare of his soul.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
The words of a whisperer are as dainty morsels, and they go down into the innermost parts.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
He also that is slack in his work is brother to him that is a destroyer.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
The name of Jehovah is a strong tower. A righteous man runs into it, and is safe.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
The rich man's wealth is his strong city, and as a high wall in his own imagination.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Before destruction the heart of man is haughty, and before honor is humility.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
He who gives answer before he hears, it is folly and shame to him.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
The spirit of a man will sustain his infirmity, but a broken spirit who can bear?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
The heart of a prudent man gets knowledge, and the ear of the wise seeks knowledge.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
A man's gift makes room for him, and brings him before great men.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
He who pleads his case first seems just, but his neighbor comes and searches him out.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
The lot causes contentions to cease, and decides between the mighty.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
A brother offended is harder to be won than a strong city, and such contentions are like the bars of a castle.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
A man's belly shall be filled with the fruit of his mouth. With the increase of his lips he shall be satisfied.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Death and life are in the power of the tongue, and those who love it shall eat the fruit of it.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
He who finds a wife finds a good thing, and obtains favor from Jehovah.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
A poor man uses entreaties, but a rich man answers roughly.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
He who makes many friends does it to his own destruction, but there is a friend who sticks closer than a brother.

< Miyambo 18 >