< Miyambo 28 >

1 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
A wicked man flees when no man pursues, but the righteous are bold as a lion.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
For the transgression of a land many are the rulers of it. But by men of understanding and knowledge the state shall be prolonged.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
A needy man who oppresses the poor is a sweeping rain which leaves no food.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
Those who forsake the law praise the wicked, but such as keep the law contend with them.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
Evil men do not understand justice, but those who seek Jehovah understand all things.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
Better is the poor man who walks in his integrity, than he who is perverse in his ways, though he be rich.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
He who keeps the law is a wise son, but he who is a companion of gluttons shames his father.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
He who augments his substance by interest and increase, gathers it for him who has pity on the poor.
9 Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
He who turns away his ear from hearing the law, even his prayer is an abomination.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
He who causes the upright to go astray in an evil way, he shall fall himself into his own pit. But the perfect shall inherit good.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
The rich man is wise in his own conceit, but a poor man who has understanding searches him out.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
When the righteous triumph, there is great glory, but when the wicked rise, men hide themselves.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
He who covers his transgressions shall not prosper, but he who confesses and forsakes them shall obtain mercy.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
Happy is the man who fears always, but he who hardens his heart shall fall into mischief.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
A roaring lion, and a ranging bear, is a wicked ruler over a poor people.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
The ruler who lacks understanding is also a great oppressor, but he who hates covetousness shall prolong his days.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
A man who is laden with the blood of any person shall flee to the pit. Let no man stay him.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
He who walks uprightly shall be delivered, but he who is perverse in his ways shall fall at once.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
He who tills his land shall have plenty of bread, but he who follows after vanity shall have poverty enough.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
A faithful man shall abound with blessings, but he who makes haste to be rich shall not be unpunished.
21 Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
To have respect of persons is not good, nor that a man should transgress for a piece of bread.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
He who has an evil eye hastens after riches, and does not know that want shall come upon him.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
He who rebukes a man shall afterward find more favor than he who flatters with the tongue.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
He who robs his father or his mother, and says, It is no transgression, the same is the companion of a destroyer.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
He who is of a greedy spirit stirs up strife, but he who puts his trust in Jehovah shall be made fat.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
He who trusts in his own heart is a fool, but he who walks wisely, he shall be delivered.
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
He who gives to the poor shall not lack, but he who hides his eyes shall have many a curse.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
When the wicked rise, men hide themselves, but when they perish, the righteous increase.

< Miyambo 28 >