< Levitiko 5 >

1 “‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
And if a soul sins, in that he hears the voice of an oath, he being a witness, whether he has seen or known, if he does not testify, then he shall bear his iniquity.
2 “‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
Or if a soul touches any unclean thing, whether it be the carcass of an unclean beast, or the carcass of unclean cattle, or the carcass of unclean creeping things, and it be hidden from him, and he be unclean, then he shall be guilty.
3 “‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
Or if he touch the uncleanness of man, whatever his uncleanness be with which he is unclean, and it be hid from him, when he knows of it, then he shall be guilty.
4 “‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
Or if a soul swears rashly with his lips to do evil, or to do good, whatever it be that a man shall utter rashly with an oath, and it be hid from him, when he realizes it, then he shall be guilty in one of these.
5 “‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
And it shall be, when he shall be guilty in one of these, that he shall confess that by which he has sinned.
6 Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
And he shall bring his trespass offering to Jehovah for his sin which he has sinned, a female from the flock, a lamb or a goat, for a sin offering. And the priest shall make atonement for him as concerning his sin.
7 “‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
And if his means is not sufficient for a lamb, then he shall bring his trespass offering for that by which he has sinned, two turtle-doves, or two young pigeons, to Jehovah, one for a sin offering, and the other for a burnt offering.
8 Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
And he shall bring them to the priest, who shall offer that which is for the sin offering first, and wring off its head from its neck, but shall not divide it apart.
9 kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
And he shall sprinkle of the blood of the sin offering upon the side of the altar, and the rest of the blood shall be drained out at the base of the altar. It is a sin offering.
10 Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
And he shall offer the second for a burnt offering, according to the ordinance. And the priest shall make atonement for him as concerning his sin which he has sinned, and he shall be forgiven.
11 “‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
But if his means is not sufficient for two turtle-doves, or two young pigeons, then he shall bring his oblation for that by which he has sinned, the tenth part of an ephah of fine flour for a sin offering. He shall put no oil upon it, nor shall he put any frankincense on it, for it is a sin offering.
12 Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
And he shall bring it to the priest, and the priest shall take his handful of it as the memorial of it, and burn it on the altar, upon the offerings of Jehovah made by fire. It is a sin offering.
13 Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
And the priest shall make atonement for him concerning his sin that he has sinned in any of these things, and he shall be forgiven. And the remnant shall be the priest's, as the meal offering.
14 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
15 “Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
If a soul commits a trespass, and sins unwittingly in the holy things of Jehovah, then he shall bring his trespass offering to Jehovah, a ram without blemish out of the flock, according to thy estimation in silver by shekels, after the shekel of the sanctuary, for a trespass offering.
16 Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
And he shall make restitution for that which he has done amiss in the holy thing, and shall add the fifth part to it, and give it to the priest. And the priest shall make atonement for him with the ram of the trespass offering, and he shall be forgiven.
17 “Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
And if a soul sins, and does any of the things which Jehovah has commanded not to be done, though he did not know it, yet he is guilty, and shall bear his iniquity.
18 Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
And he shall bring a ram without blemish out of the flock, according to thy estimation, for a trespass offering, to the priest. And the priest shall make atonement for him concerning the thing by which he erred unwittingly and knew it not, and he shall be forgiven.
19 Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”
It is a trespass offering. He is certainly guilty before Jehovah.

< Levitiko 5 >